< Psalmien 1 >

1 Autuas se mies, joka ei vaella jumalattomain neuvossa eikä astu syntisten teitä eikä istu, kussa pilkkaajat istuvat,
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 vaan rakastaa Herran lakia ja tutkistelee hänen lakiansa päivät ja yöt!
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 Hän on niinkuin istutettu puu vesiojain tykönä, joka antaa hedelmänsä ajallaan ja jonka lehti ei lakastu; ja kaikki, mitä hän tekee, menestyy.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Niin eivät jumalattomat! Vaan he ovat kuin akanat, joita tuuli ajaa.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 Sentähden eivät jumalattomat kestä tuomiolla eivätkä syntiset vanhurskasten seurakunnassa.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 Sillä Herra tuntee vanhurskasten tien, mutta jumalattomain tie hukkuu.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

< Psalmien 1 >