< Sananlaskujen 9 >

1 Viisaus on talonsa rakentanut, veistänyt seitsemän pylvästänsä.
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 Hän on teuraansa teurastanut, viininsä sekoittanut ja myöskin pöytänsä kattanut.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 Hän on palvelijattarensa lähettänyt kutsua kuuluttamaan kaupungin kumpujen rinteiltä:
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 "Joka yksinkertainen on, poiketkoon tänne". Sille, joka on mieltä vailla, hän sanoo:
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 "Tulkaa, syökää minun leipääni ja juokaa viiniä, minun sekoittamaani.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Hyljätkää yksinkertaisuus, niin saatte elää, ja astukaa ymmärryksen tielle." -
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 Joka pilkkaajaa ojentaa, saa itsellensä häpeän, ja häpeäpilkun se, joka jumalatonta nuhtelee.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 Älä nuhtele pilkkaajaa, ettei hän sinua vihaisi; nuhtele viisasta, niin hän sinua rakastaa.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Anna viisaalle, niin hän yhä viisastuu; opeta vanhurskasta, niin hän saa oppia lisää.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 Herran pelko on viisauden alku, ja Pyhimmän tunteminen on ymmärrystä. -
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 "Sillä minun avullani päiväsi enenevät ja jatkuvat elämäsi vuodet.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 Jos olet viisas, olet omaksi hyväksesi viisas; ja jos olet pilkkaaja, saat sinä sen yksin kestää."
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 Tyhmyys on nainen, levoton ja yksinkertainen, eikä hän mistään mitään tiedä.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 Hän istuu talonsa ovella, istuimella kaupungin kummuilla,
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 kutsumassa ohikulkijoita, jotka käyvät polkujansa suoraan eteenpäin:
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 "Joka yksinkertainen on, poiketkoon tänne". Ja sille, joka on mieltä vailla, hän sanoo:
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 "Varastettu vesi on makeata, ja salattu leipä on suloista".
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 Eikä toinen tiedä, että haamuja on siellä, että hänen kutsuvieraansa ovat tuonelan laaksoissa. (Sheol h7585)
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)

< Sananlaskujen 9 >