< Jesajan 35 >

1 Erämaa ja hietikko iloitsee, aromaa riemuitsee ja kukoistaa kuin lilja.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Se kauniisti kukoistaa ja iloitsee ilolla ja riemulla. Sille annetaan Libanonin kunnia, Karmelin ja Saaronin ihanuus. He saavat nähdä Herran kunnian, meidän Jumalamme ihanuuden.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Vahvistakaa hervonneet kädet, voimistakaa horjuvat polvet.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Sanokaa hätääntyneille sydämille: "Olkaa lujat, älkää peljätkö. Katso, teidän Jumalanne! Kosto tulee, Jumalan rangaistus. Hän tulee ja pelastaa teidät."
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Silloin avautuvat sokeain silmät ja kuurojen korvat aukenevat.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Silloin rampa hyppii niinkuin peura ja mykän kieli riemuun ratkeaa; sillä vedet puhkeavat erämaahan ja aromaahan purot.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 Hehkuva hiekka tulee lammikoiksi ja kuiva maa vesilähteiksi. Aavikkosutten asunnossa, missä ne makasivat, kasvaa ruoho ynnä ruoko ja kaisla.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 Ja siellä on oleva valtatie, ja sen nimi on "pyhä tie": sitä ei kulje saastainen; se on heitä itseänsä varten. Joka sitä tietä kulkee, ei eksy-eivät hullutkaan.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Ei ole siellä leijonaa, ei nouse sinne raateleva peto; ei sellaista siellä tavata: lunastetut sitä kulkevat.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Niin Herran vapahdetut palajavat ja tulevat Siioniin riemuiten, päänsä päällä iankaikkinen ilo. Riemu ja ilo saavuttavat heidät, mutta murhe ja huokaus pakenevat.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

< Jesajan 35 >