< Psalmien 135 >

1 Halleluja! Ylistäkäät Herran nimeä, kiittäkäät, Herran palveliat.
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 Te kuin seisotte Herran huoneessa, meidän Jumalamme esihuoneissa.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Kiittäkäät Herraa, sillä Herra on hyvä, ja veisatkaat kiitosta hänen nimellensä; sillä se on suloinen.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Sillä Herra on itsellensä valinnut Jakobin, Israelin omaksensa.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Minä tiedän, että Herra on suuri, ja meidän Jumalamme kaikkein jumalain ylitse.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Kaikki, mitä Herra tahtoo, niin hän tekee, taivaassa ja maassa, meressä ja kaikessa syvyydessä;
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Joka pilvet nostaa maan ääristä, joka pitkäisen leimauksesta sateen saattaa, ja tuulen tuo ulos tavaroistansa;
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Joka esikoiset Egyptissä löi, sekä ihmisistä että karjasta,
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Ja antoi merkkinsä ja ihmeensä tulla Egyptin keskelle, Pharaolle ja kaikille hänen palvelioillensa;
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Joka monet pakanat löi, ja tappoi väkevät kuninkaat:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihonin Amorilaisten kuninkaan, ja Ogin Basanin kuninkaan, ja kaikki Kanaanin valtakunnat,
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Ja antoi heidän maansa perimiseksi, Israelille kansallensa perimiseksi.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Herra, sinun nimes pysyy ijankaikkisesti: Herra, sinun muistos pysyy suvusta sukuun.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Sillä Herra tuomitsee kansansa, ja on palvelioillensa armollinen.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Pakanain epäjumalat ovat hopia ja kulta, ihmisten käsillä tehdyt.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Heillä on suu, ja ei puhu: heillä ovat silmät, ja ei näe;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Heillä ovat korvat, ja ei kuule: eikä ole henkeä heidän suussansa.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Jotka niitä tekevät, he ovat niiden kaltaiset, ja kaikki, jotka heihin uskaltavat.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Te Israelin huoneesta, kiittäkäät Herraa! te Aaronin huoneesta, kiittäkäät Herraa!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Te Levin huoneesta, kiittäkäät Herraa! te jotka Herraa pelkäätte, kiittäkäät Herraa!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Kiitetty olkoon Herra Zionista, joka Jerusalemissa asuu! Halleluja!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalmien 135 >