< Psalmien 119 >

1 Autuaat ovat ne, jotka viattomasti elävät, ja jotka Herran laissa vaeltavat.
Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2 Autuaat ovat ne, jotka hänen todistuksiansa pitävät, ja kaikesta sydämestä häntä etsivät.
Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3 Sillä, jotka hänen teissänsä vaeltavat, ei he tee mitään pahaa.
Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
4 Sinä olet käskenyt sangen visusti pitää sinun käskys.
Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5 O jospa minun tieni ojennettaisiin pitämään sinun säätyjäs!
Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
6 Koska minä katson kaikkia sinun käskyjäs, niin en minä tule häpiään.
Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
7 Minä kiitän sinua oikiasta sydämestä, ettäs opetat minulle vanhurskautes oikeudet.
Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8 Sinun säätys minä pidän, älä minua ikänä hylkää.
Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
9 Kuinka nuorukainen tiensä puhdistais? kuin hän itsensä käyttää sinun sanas jälkeen.
Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
10 Minä etsin sinua kaikesta sydämestäni: älä salli minun eksyä sinun käskyistäs.
Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11 Minä pidän sydämessäni sinun sanas, etten minä rikkoisi sinua vastaan.
Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
12 Kiitetty ole, sinä Herra: opeta minulle sinun säätyjäs!
Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
13 Minä luettelen huulillani kaikki sinun suus oikeudet.
Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
14 Minä iloitsen sinun todistustes tiellä, niinkuin kaikkinaisesta rikkaudesta.
Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15 Minä tutkistelen sinun käskyjäs, ja katselen sinun teitäs.
Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
16 Minä halajan sinun oikeuttas, ja en unohda sinun sanojas.
Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
17 Tee hyvästi palvelialles, että minä eläisin ja sinun sanas pitäisin.
Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
18 Avaa minun silmäni näkemään ihmeitä sinun laistas.
Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19 Minä olen vieras maan päällä: älä peitä minulta käskyjäs.
Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
20 Minun sieluni on muserrettu rikki ikävöitsemisestä, alati sinun oikeutes jälkeen.
Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
21 Sinä rankaiset ylpiät kirotut, jotka sinun käskyistäs poikkeevat.
Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
22 Käännä minusta pois pilkka ja ylönkatse; sillä minä pidän sinun todistukses.
Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
23 Istuvat myös päämiehet ja puhuvat minua vastaan; mutta sinun palvelias tutkistelee sinun säätyjäs.
Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24 Sinun todistukses ovat minun iloni, ne ovat minun neuvonantajani.
Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
25 Minun sieluni tomussa makaa: virvoita minua sanas jälkeen.
Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26 Minä luen minun teitäni, ja sinä kuulet minua: opeta minulle sinun säätys.
Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
27 Anna minun ymmärtää sinun käskyis tie, niin minä puhun sinun ihmeistäs.
Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28 Niin minä suren, että sydän sulaa minussa: vahvista minua sinun sanas jälkeen.
Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
29 Käännä minusta pois väärä tie, ja suo minulle sinun lakis.
Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30 Totuuden tien minä olen valinnut, oikeutes olen minä asettanut eteeni.
Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31 Minä riipun sinun todistuksissas: Herra, älä salli minun häpiään tulla.
Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32 Koskas minun sydämeni vahvistat, niin minä juoksen sinun käskyis tietä myöten.
Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
33 Opeta minulle, Herra, sinun säätyis tie, että minä sen loppuun asti kätkisin.
Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34 Anna minulle ymmärrys, kätkeäkseni sinun lakias, ja pitääkseni sitä koko sydämestäni.
Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35 Anna minun käydä sinun käskyis tietä; sillä niihin minä halajan.
Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36 Kallista minun sydämeni sinun todistuksiis, ja ei ahneuden puoleen.
Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
37 Käännä minun silmäni pois katselemasta turhuutta; vaan virvoita minua sinun tiehes.
Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38 Anna palvelias lujasti sinun käskys pitää, että minä sinua pelkäisin.
Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
39 Käännä minusta pois se pilkka, jota minä pelkään; sillä sinun oikeutes ovat suloiset.
Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
40 Katso, minä pyydän sinun käskyjäs: virvoita minua vanhurskaudellas.
Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
41 Herra, anna armos minulle tapahtua, autuutes sinun sanas jälkeen,
Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42 Että minä voisin vastata minun pilkkaajiani; sillä minä luotan sinun sanaas.
ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
43 Älä ota totuuden sanaa peräti pois minun suustani; sillä minä toivon sinun oikeuttas.
Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44 Minä pidän alati sinun lakis, aina ja ijankaikkisesti,
Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Ja vaellan ilossa, sillä minä etsin sinun käskyjäs,
Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46 Ja puhun sinun todistuksistas kuningasten edessä, ja en häpee,
Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47 Ja iloitsen sinun käskyistäs, joita minä rakastan,
popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
48 Ja nostan käsiäni sinun käskyihis, joita minä rakastan, ja puhun sinun säädyistäs.
Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
49 Muista sanaas sinun palvelialles, jota sinä annoit minun toivoa.
Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50 Tämä on minun turvani minun vaivassani, että sinun sanas virvoittaa minun.
Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51 Ylpiät irvistelevät minua sangen; en minä sentähden sinun laistas poikkee.
Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
52 Herra, kuin minä ajattelen, kuinka sinä maailman alusta toiminut olet, niin minä lohdutetaan.
Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53 Minä hämmästyin jumalattomain tähden, jotka sinun lakis hylkäävät.
Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
54 Sinun oikeutes ovat minun veisuni vaellukseni huoneessa.
Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
55 Herra, minä ajattelen yöllä sinun nimeäs, ja pidän sinun lakis.
Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56 Se olis minun tavarani, että minä sinun käskys pitäisin.
Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
57 Minä olen sanonut: Herra, se on minun perimiseni, että minä pidän sinun sanas.
Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
58 Minä rukoilen sinun kasvois edessä täydestä sydämestä: ole minulle armollinen sinun sanas jälkeen.
Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59 Minä tutkin teitäni, ja käännän jalkani sinun todistustes puoleen.
Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60 Minä riennän, ja en viivy, sinun käskyjäs pitämään.
Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
61 Jumalattomain joukko raatelee minua; mutta en minä unohda sinun lakias.
Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
62 Puoliyöstä minä nousen sinua kiittämään, sinun vanhurskautes oikeuden tähden.
Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
63 Minä olen heidän kumppaninsa, jotka sinua pelkäävät ja sinun käskyjäs pitävät,
Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64 Herra! maa on täynnä sinun hyvyyttäs: opeta minulle sinun säätyjäs.
Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
65 Hyvästi teit sinun palveliaas kohtaan, Herra, sinun sanas jälkeen.
Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
66 Opeta minulle hyviä tapoja ja taitoa; sillä minä uskon sinun käskys.
Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67 Ennenkuin minä nöyryytettiin, eksyin minä; mutta nyt minä pidän sinun sanas.
Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68 Sinä olet hyvä ja teet hyvin: opeta minulle sinun säätyjäs.
Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
69 Ylpiät ajattelevat valheen minun päälleni; mutta minä pidän täydestä sydämestä sinun käskys.
Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70 Heidän sydämensä on lihava niinkuin rasva; mutta minä iloitsen sinun laistas.
Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71 Se on minulle hyvä, ettäs minun nöyryytit, että minä sinun säätyjäs oppisin.
Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72 Sinun suus laki on minulle otollisempi kuin monta tuhatta kappaletta kultaa ja hopiaa.
Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
73 Sinun kätes ovat minun tehneet ja valmistaneet: anna minulle ymmärrystä oppiakseni sinun käskyjäs.
Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74 Jotka sinua pelkäävät, ne minun näkevät ja iloitsevat; sillä minä toivon sinun sanaas.
Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75 Herra! minä tiedän sinun tuomios vanhurskaaksi, ja sinä olet minua totuudessa nöyryyttänyt.
Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76 Olkoon siis sinun armos minun lohdutukseni, niinkuin sinä palvelialles luvannut olet.
Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77 Anna minulle sinun laupiutes tapahtua, että minä eläisin; sillä sinun lakis on minun iloni.
Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78 Jospa ylpiät häpiään tulisivat, jotka minua painavat alas valheellansa; mutta minä ajattelen sinun käskyjäs.
Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79 Tulkaan ne minun tyköni, jotka sinua pelkäävät, ja sinun todistukses tuntevat.
Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80 Olkoon minun sydämeni toimellinen sinun säädyissäs, etten minä häväistäisi.
Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
81 Minun sieluni ikävöitsee sinun autuuttas: minä toivon sinun sanas päälle.
Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82 Minun silmäni hiveltyvät sinun sanas jälkeen, ja sanovat: koskas minua lohdutat?
Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83 Sillä minä olen niinkuin nahka savussa: en minä unohda sinun säätyjäs.
Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84 Kuinka kauvan sinun palvelias odottaa? koskas tuomitset minun vainoojani?
Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85 Ylpiät minulle kuoppia kaivavat, jotka ei ole sinun lakis perään.
Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86 Kaikki sinun käskys ovat sula totuus: he valheella minua vaivaavat: auta minua.
Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87 He olisivat juuri lähes minun maan päällä hukuttaneet; mutta en minä sinun käskyjäs hyljännyt.
Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
88 Virvoita minua sinun armoillas, että minä pitäisin sinun suus todistuksen.
Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
89 Herra! sinun sanas pysyy ijankaikkisesti taivaissa.
Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
90 Sinun totuutes pysyy suvusta sukuun: sinä perustit maan, ja se pysyy.
Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91 Ne pysyvät tähän päivään asti sinun asetukses jälkeen; sillä kaikki sinua palvelevat.
Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92 Ellei sinun lakis olisi ollut minun lohdutukseni, niin minä olisin raadollisuudessani hukkunut.
Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93 En minä ikänä unohda sinun käskyjäs; sillä niillä sinä minua lohdutat.
Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94 Sinun minä olen: auta minua! sillä minä etsin sinun käskyjäs.
Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
95 Jumalattomat minua vartioitsevat hukuttaaksensa; mutta sinun todistuksistas minä otan vaarin.
Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
96 Kaikista kappaleista minä olen lopun nähnyt; mutta sinun käskys ovat määrättömät.
Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
97 Kuinka minä rakastan sinun lakias? Joka päivä minä sitä ajattelen.
Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98 Sinä teit minun taitavammaksi käskyilläs kuin minun viholliseni ovat; sillä se on minun ijankaikkinen tavarani.
Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99 Minä olen oppineempi kuin kaikki minun opettajani; sillä sinun todistukses ovat minun ajatukseni.
Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
100 Enemmän minä ymmärrän kuin vanhemmat; sillä minä pidän sinun käskys.
Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
101 Minä estän jalkani kaikista pahoista teistä, että minä sinun sanas pitäisin.
Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
102 En minä poikkee sinun oikeudestas; sillä sinä opetat minua.
Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103 Sinun sanas ovat minun suulleni makiammat kuin hunaja.
Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104 Sinun käskys tekevät minun ymmärtäväiseksi; sentähden minä vihaan kaikkia vääriä teitä.
Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
105 Sinun sanas on minun jalkaini kynttilä, ja valkeus teilläni.
Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106 Minä vannon, ja sen vahvana pidän, että minä sinun vanhurskautes oikeudet pitää tahdon.
Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107 Minä olen sangen kovin vaivattu: Herra, virvoita minua sinun sanas perästä.
Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108 Olkoon sinulle, Herra, otolliset minun suuni mieluiset uhrit, ja opeta minulle sinun oikeutes.
Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109 Minun sieluni on alati minun käsissäni, ja en unohda sinun lakias.
Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
110 Jumalattomat virittävät minulle paulan; mutta en minä eksy sinun käskyistäs.
Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111 Sinun todistukses ovat minun ijankaikkiset perimiseni; sillä ne ovat minun sydämeni ilo.
Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112 Minä kallistan minun sydämeni tekemään sinun säätys jälkeen, aina ja ijankaikkisesti.
Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
113 Minä vihaan viekkaita henkiä, ja rakastan sinun lakias.
Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
114 Sinä olet minun varjelukseni ja kilpeni: minä toivon sinun sanas päälle.
Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115 Poiketkaat minusta, te pahanilkiset; ja minä pidän minun Jumalani käskyt.
Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116 Tue minua sanallas, että minä eläisin, ja älä anna minun toivoni häpiään tulla.
Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117 Vahvista minua, että minä autetuksi tulisin, niin minä halajan alati sinun säätyjäs.
Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118 Sinä tallaat alas kaikki, jotka sinun säädyistäs horjuvat; sillä heidän viettelyksensä on sula valhe.
Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119 Sinä heität pois kaikki jumalattomat maan päältä niinkuin loan; sentähden minä rakastan sinun todistuksias.
Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120 Minä pelkään sinua, niin että minun ihoni värisee, ja vapisen sinun tuomioitas.
Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
121 Minä teen oikeuden ja vanhurskauden: älä minua hylkää niille, jotka minulle väkivaltaa tekevät.
Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122 Vastaa palvelias edestä, ja lohduta häntä, ettei ylpiät tekisi minulle väkivaltaa.
Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123 Minun silmäni hiveltyvät sinun autuutes perään, ja sinun vanhurskautes sanan jälkeen.
Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124 Tee palvelias kanssa sinun armos jälkeen, ja opeta minulle sinun säätyjäs.
Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125 Sinun palvelias minä olen: anna minulle ymmärrystä, että minä tuntisin sinun todistukses.
Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126 Jopa aika on, että Herra siihen jotakin tekis: he ovat sinun lakis särkeneet.
Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
127 Sentähden minä rakastan sinun käskyjäs, enempi kuin kultaa ja parasta kultaa.
Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128 Sentähden minä pidän visusti kaikkia sinun käskyjäs: minä vihaan kaikkia vääriä teitä.
ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
129 Ihmeelliset ovat sinun todistukses; sentähden minun sieluni ne pitää.
Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130 Kuin sinun sanas julistetaan, niin se valistaa ja antaa yksinkertaisille ymmärryksen.
Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131 Minä avaan suuni ja huokaan; sillä minä halajan sinun käskys.
Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
132 Käännä sinuas minun puoleeni, ja ole minulle armollinen, niinkuin sinä olet niille tottunut tekemään, jotka sinun nimeäs rakastavat.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133 Vahvista minun käymiseni sinun sanassas, ja älä anna väkivallan minua vallita.
Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134 Lunasta minua ihmisten väkivallasta, niin minä pidän sinun käskys.
Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135 Valista sinun kasvos palvelias päälle, ja opeta minulle sinun säätys.
Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136 Minun silmäni vettä vuotavat, niinkuin virta, ettei sinun käskyjäs pidetä.
Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
137 Herra! sinä olet vanhurskas ja sinun tuomios ovat oikiat.
Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
138 Sinä olet vanhurskautes todistukset ja totuuden visusti käskenyt.
Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
139 Minä olen lähes surmakseni kiivannut, että minun viholliseni ovat sinun sanas unohtaneet.
Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140 Sinun puhees on sangen koeteltu, ja sinun palvelias sen rakkaana pitää.
Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141 Minä olen halpa ja ylönkatsottu, mutta en minä unohda sinun käskyjäs.
Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
142 Sinun vanhurskautes on ijankaikkinen vanhurskaus, ja sinun lakis on totuus.
Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
143 Ahdistus ja tuska ovat minun saavuttaneet; mutta minä iloitsen sinun käskyistäs.
Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144 Sinun todistustes vanhurskaus pysyy ijankaikkisesti: anna minulle ymmärrys, niin minä elän.
Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
145 Minä huudan kaikesta sydämestäni: kuule, Herra, minua, että minä sinun säätys pitäisin.
Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146 Sinua minä huudan, auta minua, että minä sinun todistukses pitäisin.
Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147 Varhain minä ennätän, ja huudan: sinun sanas päälle minä toivon.
Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148 Varhain minä herään, tutkistelemaan sinun sanojas.
Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149 Kuule minun ääneni sinun armos jälkeen: Herra, virvoita minua sinun oikeutes jälkeen.
Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150 Pahanilkiset vainoojat karkaavat minun päälleni, ja ovat kaukana sinun laistas.
Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
151 Herra, sinä olet läsnä, ja sinun käskys ovat sula totuus.
Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
152 Mutta minä sen aikaa tiesin, että sinä olet todistukses ijankaikkisesti perustanut.
Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
153 Katso minun raadollisuuttani, ja pelasta minua; sillä enpä minä unohda sinun lakias.
Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154 Toimita minun asiani ja päästä minua: virvoita minua sinun sanas kautta.
Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155 Autuus on kaukana jumalattomista, sillä ei he tottele säätyjäs.
Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156 Herra, sinun laupiutes on suuri: virvoita minua sinun oikeutes jälkeen.
Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157 Minun vainoojaani ja vihollistani on monta; mutta en minä poikkee sinun todistuksistas.
Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158 Minä näen ylönkatsojat, ja siihen suutun, ettei he sinun sanaas pidä.
Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
159 Katso, minä rakastan sinun käskyjäs: Herra, virvoita minua sinun armos jälkeen.
Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160 Sinun sanas on alusta totuus ollut: kaikki sinun vanhurskautes oikeudet pysyvät ijankaikkisesti.
Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
161 Päämiehet vainoovat minua ilman syytä; mutta minun sydämeni pelkää sinun sanojas.
Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162 Minä iloitsen sinun puheestas, niinkuin se joka suuren saaliin löytänyt on.
Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163 Valhetta minä vihaan ja kauhistun; mutta sinun lakias minä rakastan.
Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
164 Seitsemästi päivässä minä kiitän sinua sinun vanhurskautes oikeuden tähden.
Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
165 Suuri rauha on niillä, jotka sinun lakias rakastavat, ja ei he itsiänsä loukkaa.
Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166 Herra! minä odotan sinun autuuttas, ja teen sinun käskys.
Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167 Minun sieluni pitää sinun todistukses, ja minä rakastan niitä sangen suuresti.
Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
168 Minä pidän sinun käskys ja todistukses; sillä kaikki minun tieni ovat edessäs.
Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
169 Herra! anna minun huutoni tulla sinun etees: anna minulle ymmärrystä sinun sanas jälkeen.
Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170 Anna minun rukoukseni tulla sinun etees: pelasta minua sinun sanas jälkeen.
Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171 Minun huuleni kiittävät, koskas minulle opetat sinun säätys.
Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172 Minun kieleni puhuu sinun sanastas; sillä kaikki sinun käskys ovat vanhurskaat.
Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173 Olkoon sinun kätes minulle avullinen; sillä minä olen valinnut sinun käskys.
Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
174 Herra, minä ikävöitsen sinun autuuttas, ja halajan sinun lakias.
Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175 Anna minun sieluni elää, että hän sinua kiittäis, ja sinun oikeutes auttakoon minua!
Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
176 Minä olen eksyvä niinkuin kadotettu lammas, etsi sinun palveliaas; sillä en minä unohda sinun käskyjäs.
Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Psalmien 119 >