< Psalmien 114 >

1 Kuin Israel Egyptistä läksi, Jakobin huone muukalaisesta kansasta,
Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
2 Niin Juuda tuli hänen pyhäksensä: Israel hänen vallaksensa.
Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
3 Sen meri näki ja pakeni: Jordan palasi takaperin,
Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
4 Vuoret hyppäsivät niinkuin oinaat, ja kukkulat niinkuin nuoret lampaat.
mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
5 Mikä sinun oli meri, ettäs pakenit? ja sinä Jordan, ettäs palasit takaperin?
Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
6 Te vuoret, että te hyppäsitte niinkuin oinaat? te kukkulat niinkuin nuoret lampaat?
inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
7 Herran edessä vapisi maa, Jakobin Jumalan edessä,
Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
8 Joka kalliot muuttaa vesilammiksi, ja kiven vesilähteeksi.
amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.

< Psalmien 114 >