< Sananlaskujen 29 >
1 Joka kuritukselle on uppiniskainen, hän äkisti kadotetaan ilman yhdetäkään avuta.
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 Kuin vanhurskaita monta on, niin kansa iloitsee; vaan kuin jumalatoin hallitsee, niin kansa huokaa.
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 Joka viisautta rakastaa, hän iloittaa isänsä; mutta joka huoria elättää, hän tuhlaa tavaraansa.
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 Kuningas rakentaa oikeudella valtakunnan; vaan lahjain ottaja sen turmelee.
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 Joka lähimmäisensä kanssa liehakoitsee, hän hajoittaa verkon jalkainsa eteen.
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 Kuin paha syntiä tekee, niin hän hänensä paulaan sekoittaa; vaan vanhurskas riemuitsee, ja hänellä on ilo.
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 Vanhurskas tuntee köyhän asian; vaan jumalatoin ei ymmärrä viisautta.
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 Pilkkaajat hajoittavat kaupungin; vaan viisaat asettavat vihan.
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 Kuin viisas tulee tyhmän kanssa oikeutta käymään, joko hän on vihainen eli iloinen, niin ei ole hänellä yhtään lepoa.
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 Verikoirat vihaavat siviää; vaan vanhurskaat holhovat häntä.
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 Tyhmä vuodattaa kaiken henkensä; vaan viisas sen pidättää.
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 Päämies, joka valhetta rakastaa, hänen palveliansa ovat kaikki jumalattomat.
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 Köyhä ja rikas kohtasivat toinen toisensa: Herra valaisee heidän molempain silmänsä.
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 Kuningas, joka uskollisesti tuomitsee köyhiä, hänen istuimensa vahvistetaan ijankaikkisesti.
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 Vitsa ja rangaistus antaa viisauden; vaan itsevaltainen lapsi häpäisee äitinsä.
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 Jossa monta jumalatointa on, siinä on monta syntiä; vaan vanhurskaat näkevät heidän lankeemisensa.
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 Kurita poikaas, niin hän sinua virvoitaa, ja saattaa sielus iloiseksi.
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 Kuin ennustukset loppuvat, niin kansa hajoitetaan; vaan autuas kätkee lain.
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 Palvelia ei anna itsiänsä kurittaa sanoilla; sillä vaikka hän sen ymmärtää, niin ei hän vastaa.
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 Jos sinä näet jonkun, joka on nopsa puhumaan: enempi on toivoa tyhmästä kuin hänestä.
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 Jos palvelia nuoruudesta herkullisesti pidetään, niin hän tahtoo sitte poikana olla.
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 Vihainen mies saattaa riidan, ja kiukkuinen tekee monta syntiä.
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 Ylpeys kukistaa ihmisen; vaan kunnia korottaa nöyrän.
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 Joka varkaan kanssa on osallinen, hän vihaa sieluansa, niin myös se, joka kuulee kirouksen ja ei ilmoita.
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 Joka pelkää ihmistä, hän tulee lankeemukseen; mutta joka luottaa Herraan, hän tulee pidetyksi ylös.
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 Moni etsii päämiehenkasvoja; mutta jokaisen tuomio tulee Herralta.
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 Jumalatoin ihminen on vanhurskaille kauhistus; ja joka oikialla tiellä on, hän on jumalattomalle kauhistus.
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.