< Sananlaskujen 2 >

1 Poikani, jos otat minun puheeni, ja käskyni kätket;
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 Niin anna korvas kuulla viisautta, ja taivuta sydämes ymmärrykseen.
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 Sillä jos ymmärrystä ahkerasti halajat, ja rukoilet taitoa;
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 Jos sitä etsit niinkuin hopiaa, ja pyörit sen perään niinkuin tavaran;
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Niin sinä ymmärrät Herran pelvon, ja Herran tunnon löydät.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 Sillä Herra antaa viisauden, ja hänen suustansa tulee taito ja ymmärrys.
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Hän antaa toimellisten hyvin käydä, ja suojelee niitä, jotka viattomasti vaeltavat,
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 Varjelee hurskaat, ja holhoo pyhäinsä retket.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Silloin sinä ymmärrät vanhurskauden ja tuomion, oikeuden ja kaiken hyvän tien.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 Jos viisaus sydämees tulee, ja taito on sinulle kelvollinen,
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Niin hyvä neuvo sinua varjelee, ja ymmärrys kätkee sinun,
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 Tempaamaan sinun pois pahalta tieltä, ja niiden seurasta, jotka toimettomia puhuvat,
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 Ja hylkäävät oikian tien, ja vaeltavat pimeitä retkiä;
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Jotka iloitsevat pahoista töistänsä, ja riemuitsevat pahoista menoistansa;
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Joiden tiet ovat vastahakoiset, ja retket väärär ja häpiälliset:
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 Ettet sinä ryhtyisi vieraaseen vaimoon, joka ei sinun ole, joka suloisilla sanoilla puhuttelee,
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Ja hylkää nuoruutensa johdattajan, ja unohtaa Jumalansa liiton.
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 Sillä hänen huoneensa kallistuu kuolemaan, ja hänen askeleensa kadotettuin tykö.
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 Jokainen joka menee hänen tykönsä, ei palaja, eikä elämän tielle joudu;
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 Ettäs vaeltasit hyvää tietä, ja pitäisit hurskasten tiet.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 Sillä vanhurskaat asuvat maassa, ja vakaat siinä pysyvät;
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 Mutta jumalattomat hukutetaan maasta, ja ylönkatsojat siitä teloitetaan.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

< Sananlaskujen 2 >