< 4 Mooseksen 29 >

1 Ensimäisenä päivänä seitsemännellä kuukaudella pitää teillä pyhä kokous oleman: ei yhtään orjan työtä pidä teidän (silloin) tekemän: se pitää oleman soittamisen juhlapäivä.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Ja teidän pitää uhraaman polttouhria makiaksi hajuksi Herralle: yhden nuoren mullin, yhden oinaan, seitsemän vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä,
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 Niin myös heidän ruokauhrinsa: öljyllä sekoitettuja sämpyläjauhoja, kolme kymmenestä mullille, kaksi kymmenestä oinaalle,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 Ja yhden kymmeneksen jokaiselle karitsalle, niistä seitsemästä karitsasta,
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 Ja yhden kauriin syntiuhriksi, teitä sovittamaan,
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 Paitsi saman kuukauden polttouhria ja ruokauhria, ja paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa, heidän säätynsä jälkeen makian hajun tuleksi Herralle.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 Kymmenentenä päivänä tällä seitsemännellä kuukaudella pitää myös teillä pyhä kokous oleman ja teidän pitää vaivaaman teidän sielujanne, ja ei yhtään työtä (silloin) tekemän.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Vaan teidän pitää uhraaman polttouhria makiaksi hajuksi Herralle: yhden nuoren mullin, ja yhden oinaan, ja seitsemän vuosikuntaista karitsaa: virheettömät ne pitää oleman teillä,
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 Ynnä heidän ruokauhrinsa kanssa: sämpyläjauhoja, sekoitettuja öljyllä, kolme kymmenestä mullille, kaksi kymmenestä oinaalle,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 Ja aina kymmeneksen jokaiselle karitsalle, niistä seitsemästä karitsasta,
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 Yhden kauriin syntiuhriksi, paitsi sovittamisen syntiuhria ja alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 Viidentenätoistakymmenentenä päivänä seitsemännellä kuukaudella pitää teillä pyhä kokous oleman: ei mitään orjan työtä pidä teidän (silloin) tekemän, ja teidän pitää juhlaa pitämän Herralle ne seitsemän päivää.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Ja teidän pitää uhraaman polttouhria ja tuliuhria, makiaksi hajuksi Herralle: kolmetoistakymmentä nuorta mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa: virheettömät ne pitää oleman,
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 Heidän ruokauhrinsa kanssa, sämpyläjauhoja, sekoitettuja öljyllä, kolme kymmenestä jokaiselle kolmestatoistakymmenestä mullista, kaksi kymmenestä kumpaisellekin oinaalle.
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 Ja kymmeneksen itsekullekin neljästätoistakymmenestä karitsasta,
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 Siihen myös kauriin syntiuhriksi: paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 Ja toisena päivänä kaksitoistakymmentä nuorta mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä,
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 Ja heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä perästä.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 Siihen myös kauriin syntiuhriksi: paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 Kolmantena päivänä yksitoistakymmentä mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä.
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 Ja heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä jälkeen.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 Siihen myös kauriin syntiuhriksi: paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 Neljäntenä päivänä kymmenen mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä,
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 Heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä jälkeen.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 Siihen kauriin syntiuhriksi; paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 Ja viidentenä päivänä yhdeksän mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa, ilman virhettä.
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 Ja heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä jälkeen.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 Siihen myös kauriin syntiuhriksi; paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 Ja kuudentena päivänä kahdeksan mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 Ja heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä jälkeen.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 Siihen myös kauriin syntiuhriksi; paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 Ja seitsemäntenä päivänä seitsemän mullia, kaksi oinasta, neljätoistakymmentä vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 Ja heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä jälkeen.
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 Siihen myös kauriin syntiuhriksi; paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 Kahdeksas päivä pitää oleman teille päätösjuhla: ei yhtään orjan työtä teidän pidä (silloin) tekemän.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Ja teidän pitää uhraaman polttouhria makian hajun tuleksi Herralle: yhden mullin, yhden oinaan ja seitsemän vuosikuntaista karitsaa, virheetöinnä,
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 Heidän ruokauhrinsa ja juomauhrinsa mulleille, oinaille ja karitsoille, heidän lukunsa ja säätynsä jälkeen.
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 Siihen myös kauriin syntiuhriksi; paitsi alinomaista polttouhria, ruokauhrinensa ja juomauhrinensa.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Nämät pitää teidän tekemän Herralle juhlapäivinänne, paitsi mitä te mielellänne lupaatte ja hyvällä tahdollanne annatte polttouhriksenne, ruokauhriksenne, juomauhriksenne ja kiitosuhriksenne.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Ja Moses sanoi Israelin lapsille kaikki ne, mitä Herra hänelle käskenyt oli.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< 4 Mooseksen 29 >