< Johannes 1 >

1 Alguses oli Sõna juba olemas. Sõna oli Jumala juures ja Sõna oli Jumal.
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 Alguses oli ta Jumala juures.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 Kõik on tekkinud tema kaudu; ilma temata ei ole tekkinud midagi.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 Temas oli elu, see elu, mis on kõigi valgus.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 Valgus paistab pimedusse ja pimedus ei ole seda kustutanud.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 Jumal saatis mehe nimega Johannes.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 Ta tuli tunnistajana selgitama valgust, et kõik võiksid tema kaudu uskuda.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 Tema ise ei olnud valgus, vaid ta tuli valgusest tunnistama.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 Tõeline valgus oli tulemas maailma, et valgustada kõiki.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 Ta oli maailmas, ja kuigi maailm oli tehtud tema kaudu, ei tundud maailm, kes ta on.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 Ta tuli omade juurde, kuid nad ei võtnud teda omaks.
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 Kuid kõigile neile, kes ta vastu võtsid ja temasse uskusid, andis ta õiguse saada Jumala lapseks.
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 Need lapsed ei ole sündinud tavalisel moel, mitte inimese soovi või isa otsuse tulemusena, vaid nad on sündinud Jumalast.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 Sõna sai inimeseks ja elas meie keskel ning me nägime tema au, Isa ühe ja ainsa Poja au, täis armu ja tõde.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 Johannes tunnistas temast, hüüdes rahvale: „See on tema, kellest ma teile rääkisin, kui ütlesin: „See, kes tuleb pärast mind, on minust tähtsam, sest tema oli olemas juba enne mind.““
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 Me kõik oleme saanud osa tema heldusest, ühe armulise kingi teise järel.
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 Seadus anti Moosese kaudu; arm ja tõde tulid Jeesuse Kristuse kaudu.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 Kuigi keegi ei ole eales Jumalat näinud, on üks ja ainus Jumal, kes on Isa lähedal, näidanud meile, missugune on Jumal.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 Seda teatas Johannes avalikult, kui juudi juhid saatsid Jeruusalemmast preestreid ja leviite temalt küsima: „Kes sa oled?“
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 Johannes kuulutas lihtsalt ja selgelt, ilma kõhklemata: „Ma ei ole Messias.“
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 „Kes sa siis oled?“küsisid nad. „Kas Eelija?“„Ei, ei ole, “vastas ta. „Kas sa oled see prohvet?“„Ei, “kostis ta.
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 „Kes sa siis oled?“küsisid nad. „Me peame andma vastuse neile, kes meid saatsid. Mida sa enda kohta ütled?“
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 „Ma olen hääl, mis hüüab kõrbes: „Tehke Issanda tee sirgeks!““ütles ta prohvet Jesaja sõnu kasutades.
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 Variseride saadetud preestrid ja leviidid
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 küsisid talt: „Miks sa siis ristid, kui sa ei ole Messias, Eelija ega see prohvet?“
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 Johannes vastas: „Mina ristin veega, kuid teie keskel seisab see, keda te ei tunne.
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 Tema tuleb pärast mind, aga ma ei ole väärt isegi tema sandaale lahti päästma.“
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 See kõik toimus teiselpool Jordanit Betaanias, kus Johannes ristis.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 Järgmisel päeval nägi Johannes Jeesust lähenemas ja ütles: „Vaadake, Jumala Tall, kes võtab ära maailma patu!
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 Tema on see, kellest ma rääkisin, kui ütlesin: „Pärast mind tuleb minust tähtsam mees, sest tema oli olemas juba enne mind.“
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 Ma ise ei teadnud, kes ta on, kuid mina tulin ristima veega, et tema saaks Iisraelile ilmutatud.“
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 Johannes andis tunnistust temast, öeldes: „Ma nägin taevast laskumas Vaimu nagu tuvi ja tema peale jäämas.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 Ma ei oleks teda tundud, kui see, kes läkitas mind veega ristima, ei oleks mulle öelnud: „See, kelle peale sa näed Vaimu laskumas ja sinna jäämas, on see, kes ristib Püha Vaimuga.“
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 Ma nägin seda toimumas ja kinnitan, et see on Jumala Poeg.“
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 Järgmisel päeval seisis Johannes koos oma kahe jüngriga.
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 Ta nägi Jeesust mööda minemas ja ütles: „Vaadake! See on Jumala Tall!“
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 Kui kaks jüngrit kuulsid tema sõnu, läksid nad ja järgisid Jeesust.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 Jeesus pöördus ja nägi neid järgnemas. „Mida te otsite?“küsis ta neilt. „Rabi (mis tähendab „Õpetaja“), kus sa peatud?“küsisid nad vastu.
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 „Tulge ja vaadake, “ütles ta neile. Nii nad siis läksid koos temaga ja nägid, kus ta peatus. Kell oli umbes neli pärastlõunal, ja nad veetsid ülejäänud päeva temaga koos.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 Andreas, Siimon Peetruse vend, oli üks neist kahest jüngrist, kes olid kuulnud, mida Johannes ütles, ja oli Jeesust järginud.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 Ta läks kohe otsima oma venda Siimonat ja ütles talle: „Me leidsime Messia!“(mis tähendab „Kristus“).
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 Ta viis tema Jeesuse juurde. Siimonale otsa vaadates ütles Jeesus: „Sina oled Siimon, Johannese poeg. Aga nüüd hüütakse sind Keefaseks“(mis tähendab „Peetrus“).
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 Järgmisel päeval otsustas Jeesus minna Galileasse. Jeesus leidis sealt Filippuse ja ütles talle: „Järgne mulle.“
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 Filippus oli pärit Betsaidast, samast linnast, kust Andreas ja Peetruski.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 Filippus leidis Naatanaeli ja ütles talle: „Me leidsime tema, kellest Mooses kirjutas seaduses ja ka prohvetid − Naatsaretist pärit Jeesuse, Joosepi poja.“
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 „Naatsaretist? Kas sealt saab tulla midagi head?“imestas Naatanael. „Lihtsalt tule ja vaata, “vastas Filippus.
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 Kui Jeesus nägi Naatanaeli lähenemas, ütles ta tema kohta: „Vaadake, siin on õige iisraellane! Temas ei ole midagi väärat.“
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 „Kuidas sa tead, kes ma olen?“küsis Naatanael. „Ma nägin sind seal viigipuu all, enne kui Filippus sind kutsus, “vastas Jeesus.
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 „Rabi, sina oled Jumala Poeg, Iisraeli kuningas!“hüüatas Naatanael.
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 „Kas sa usud seda lihtsalt sellepärast, et ma ütlesin sulle, et nägin sind viigipuu all?“ütles Jeesus. „Sa saad näha veel palju rohkem kui see!“
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 Seejärel lausus Jeesus: „Ma räägin teile tõtt: te kõik näete taeva olevat avatud ja Jumala inglid käimas üles ja alla inimese Poja peal.“
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

< Johannes 1 >