< Ijob 34 >
1 Elihu parolis plue, kaj diris:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Aŭskultu, saĝuloj, miajn vortojn; Kaj vi, kompetentuloj, atentu min.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Ĉar la orelo esploras la parolon, Kiel la palato gustumas la manĝaĵon.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Decidon ni elektu al ni; Ni esploru inter ni, kio estas bona.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 Ĉar Ijob diris: Mi estas prava, Sed Dio forigis mian rajton;
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 En mia juĝa afero mi estas refutata; Turmentas min mia sago, kvankam mi estas senkulpa.
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Kiu homo estas simila al Ijob, Kiu trinkas mokojn kiel akvon?
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Kaj li estas preta aliĝi al malbonaguloj Kaj iri kun malpiuloj;
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Ĉar li diras: Homo ne havas utilon, Se li serĉas favoron de Dio.
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Tial aŭskultu min, ho saĝaj homoj: Dio estas malproksima de malbonagoj, Kaj la Plejpotenculo estas malproksima de maljusteco;
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Sed Li repagas al homo laŭ liaj agoj, Kaj laŭ la vojo de ĉiu Li renkontas lin.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Vere, Dio ne malbonagas, Kaj la Plejpotenculo ne kurbigas la veron.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Kiu komisiis al Li la teron? Kaj kiu starigis Lin super la tuta mondo?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 Se Li pensus nur pri Si, Se Li prenus al Si Sian spiriton kaj spiron,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 Tiam pereus absolute ĉiu karno, Kaj homo refariĝus polvo.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 Se vi havas prudenton, aŭskultu ĉi tion; Atentu la voĉon de miaj paroloj.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Ĉu povas regi malamanto de justeco? Ĉu vi povas akuzi la Plejjustulon?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Ĉu oni povas diris al reĝo: Sentaŭgulo; Aŭ al altranguloj: Malpiulo?
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Sed Li ne atentas la vizaĝon de princoj, Kaj ne preferas riĉulon antaŭ malriĉulo; Ĉar ĉiuj estas faritaĵo de Liaj manoj.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 Momente ili mortas, noktomeze ili tumultiĝas kaj malaperas; Ne de homa mano estas forigataj la potenculoj.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 Ĉar Liaj okuloj estas super la vojoj de homo, Kaj ĉiujn liajn paŝojn Li vidas.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 Ne ekzistas mallumo nek ombrego, Kie povus sin kaŝi malbonaguloj.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Li ne bezonas multe klopodi kun homo, Ke li iru al Dio por juĝo.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Li pereigas la fortulojn sennombre Kaj starigas sur ilia loko aliajn;
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Ĉar Li scias iliajn farojn; Li renversas ilin en la nokto, kaj ili frakasiĝas.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Kiel malpiulojn Li frapas ilin sur loko, kie ĉiuj vidas;
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Pro tio, ke ili forturniĝis de Li Kaj ne penis kompreni ĉiujn Liajn vojojn,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 Sed venigis al Li la kriadon de malriĉulo, Kaj Li aŭdis la kriadon de mizeruloj.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Se Li kvietigas, tiam kiu povas ribeligi? Se Li kaŝas Sian vizaĝon, tiam kiu povas Lin vidi? Tiel estas egale kun nacio kaj kun aparta homo,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 Por ke ne regu homo hipokrita, El la pekigantoj de popolo.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 Al Dio oni devas diri: Mi fieriĝis, mi ne plu faros malbonon;
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Kion mi ne vidas, pri tio instruu min; Se mi faris maljustaĵon, mi ne plu faros.
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Ĉu konforme al via opinio Li devas repagi? Al vi ja ne plaĉis. Vi elektu, ne mi; Kaj kion vi scias, tion diru.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Saĝaj homoj diros al mi, Kaj prudenta homo, kiu min aŭskultas:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 Ijob parolas malsaĝe, Kaj liaj vortoj estas malprudentaj.
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Ho, se Ijob estus elprovita ĝis la fino, Pro tio, ke li aliĝas al homoj pekaj;
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Ĉar al sia peko li aldonas blasfemon; Inter ni li mokas, kaj multe parolas kontraŭ Dio.
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”