< Ijob 30 >

1 Sed nun ridas pri mi homoj pli junaj ol mi, Kies patrojn mi ne volus starigi kun la hundoj de miaj ŝafaroj;
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Kies forto de la manoj estis senbezona por mi, Kaj kiuj ne povis atingi maljunecon;
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Kiuj pro malriĉeco kaj malsato solece kuris En la dezerton mizeran kaj senvivan;
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Kiuj elŝiras atriplon apud la arbetaĵoj, Kaj kies pano estas la radiko de genisto.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 El meze de la homoj oni elpelas ilin; Oni krias sur ilin, kiel sur ŝteliston;
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 En terfendoj ĉe la valoj ili loĝas, En truoj de la tero kaj de rokoj;
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 Inter la arbetaĵoj ili krias, Sub la kardoj ili kolektiĝas;
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Kiel infanoj de sentaŭguloj kaj sennomuloj, Ili estas elpelitaj el la lando.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 Kaj nun mi fariĝis objekto de ilia mokokanto, Mi fariĝis por ili objekto de babilado.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Ili abomenas min, malproksimiĝas de mi, Ne timas kraĉi sur mian vizaĝon.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Li malligis mian ŝnuron kaj turmentas min, Kaj ili forĵetis antaŭ mi la bridon.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 Dekstre buboj stariĝis, kaj puŝas miajn piedojn; Ili ebenigis kontraŭ mi siajn pereigajn vojojn;
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Ili disfosis mian vojon, facile pereigas min, Ne bezonante helpanton;
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Ili venas kiel tra larĝa breĉo, Ĵetas sin tumulte.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Teruroj turnis sin kontraŭ min, Forpelis mian majeston kiel vento; Kiel nubo foriris mia feliĉo.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 Kaj nun elverŝiĝas mia animo; Kaptis min tagoj de mizero.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 En la nokto miaj ostoj traboriĝas en mi, Kaj miaj mordetantoj ne dormas.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Kun granda malfacileco demetiĝas mia vesto; Premas min la rando de mia ĉemizo.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Oni komparas min kun koto; Mi similiĝis al polvo kaj cindro.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 Mi krias al Vi, sed Vi ne respondas al mi; Mi staras, ke Vi atentu min.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Vi fariĝis kruelulo por mi; Per la forto de Via mano Vi montras al mi Vian malamon.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Vi levis min en la venton, Lasis min kaj neniigis min en la ventego.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Mi scias, ke Vi transdonos min al la morto, En la kunvenejon de ĉio vivanta.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Sed ĉu oni povas ne deziri eltiri manon, Kaj krii en sia malfeliĉo?
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Ĉu mi ne ploris pri tiu, kiu havis malfeliĉan tempon? Ĉu mia animo ne afliktiĝis pri malriĉulo?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Mi atendis bonon, sed venis malbono; Mi esperis lumon, sed venis mallumo.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Miaj internaĵoj bolas kaj ne ĉesas; Atakis min tempo de mizero.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Mi estas nigra, sed ne de la suno; Mi leviĝas en la komunumo kaj krias.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Mi fariĝis frato al la ŝakaloj Kaj kamarado al la strutoj.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Mia haŭto nigriĝis sur mi, Kaj miaj ostoj sekiĝis de varmego.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Mia harpo fariĝis plendilo, Kaj mia fluto fariĝis voĉo de plorantoj.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Ijob 30 >