< Ijob 20 >
1 Ekparolis Cofar, la Naamano, kaj diris:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Pro tio miaj pensoj devigas min respondi, Pro tio, kion mi sentas.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 Hontindan riproĉon mi aŭdis, Kaj la spirito de mia prudento respondos por mi.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Ĉu vi scias, ke tiel estis de eterne, De post la apero de homo sur la tero,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 Ke la triumfado de malvirtuloj estas mallongatempa, Kaj la ĝojo de hipokritulo estas nur momenta?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Se lia grandeco eĉ atingus ĝis la ĉielo, Kaj lia kapo tuŝus la nubon,
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 Li tamen pereos por ĉiam, kiel lia sterko; Tiuj, kiuj lin vidis, diros: Kie li estas?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Kiel sonĝo li forflugos, kaj oni lin ne trovos; Li malaperos, kiel nokta vizio.
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 Okulo, kiu rigardis lin, ne plu vidos lin; Lia loko lin ne plu vidos.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Liaj filoj kurados almozpetante, Kaj liaj manoj redonos lian havaĵon.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Liaj ostoj estos punitaj pro la pekoj de lia juneco, Kaj tio kuŝiĝos kune kun li en la polvo.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Se la malbono estas dolĉa en lia buŝo, Li kaŝas ĝin sub sia lango,
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 Li flegas ĝin kaj ne forlasas ĝin, Kaj retenas ĝin sur sia palato:
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 Tiam lia manĝaĵo renversiĝos en liaj internaĵoj, Fariĝos galo de aspidoj interne de li.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Li englutis havaĵon, sed li ĝin elvomos; El lia ventro Dio ĝin elpelos.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Venenon de aspidoj li suĉos; Lango de vipuro lin mortigos.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 Li ne vidos fluojn nek riverojn, Torentojn de mielo kaj de butero.
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Li redonos tion, kion li pene akiris, kaj li tion ne englutos; Kiel ajn granda estas lia havaĵo, li ĝin fordonos kaj ne ĝuos ĝin.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Ĉar li premis kaj forlasis la senhavulojn, Li rabis al si domon, kiun li ne konstruis.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Ĉar lia interno ne estis trankvila, Tial li ne savos tion, kio estis por li kara.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Nenion restigis lia manĝemeco; Tial lia bonstato ne estos longedaŭra.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 Malgraŭ lia abundeco, li estos premata; Ĉiaspecaj suferoj trafos lin.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 Por plenigi lian ventron, Li sendos sur lin la flamon de Sia kolero, Kaj pluvigos sur lin Sian furiozon.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 Se li forkuros de batalilo fera, Trafos lin pafarko kupra.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 Nudigita glavo trairos lian korpon, Kaj la fulmo de lia turmentilo venos sur lin kun teruro.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 Nenia mallumo povos kaŝi liajn trezorojn; Lin konsumos fajro ne disblovata; Malbone estos al tiu, kiu restos en lia tendo.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 La ĉielo malkovros liajn malbonagojn, Kaj la tero leviĝos kontraŭ lin.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Malaperos la greno el lia domo, Disŝutita ĝi estos en la tago de Lia kolero.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Tia estas de Dio la sorto de homo malpia, Kaj la heredaĵo destinita por li de Dio.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”