< Psalms 99 >
1 Jehovah hath reigned, peoples tremble, The Inhabitant of the cherubs, the earth shaketh.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Jehovah in Zion [is] great, And high He [is] over all the peoples.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 They praise Thy name, 'Great, and fearful, holy [it] is.'
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 And the strength of the king Hath loved judgment, Thou — Thou hast established uprightness; Judgment and righteousness in Jacob, Thou — Thou hast done.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Exalt ye Jehovah our God, And bow yourselves at His footstool, holy [is] He.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moses and Aaron among His priests, And Samuel among those proclaiming His name. They are calling unto Jehovah, And He doth answer them.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 In a pillar of cloud He speaketh unto them, They have kept His testimonies, And the statute He hath given to them.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 O Jehovah, our God, Thou hast afflicted them, A God forgiving Thou hast been to them, And taking vengeance on their actions.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Exalt ye Jehovah our God, And bow yourselves at His holy hill, For holy [is] Jehovah our God!
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.