< Psalms 90 >
1 A Prayer of Moses, the man of God. Lord, a habitation Thou — Thou hast been, To us — in generation and generation,
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Before mountains were brought forth, And Thou dost form the earth and the world, Even from age unto age Thou [art] God.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Thou turnest man unto a bruised thing, And sayest, Turn back, ye sons of men.
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 For a thousand years in Thine eyes [are] as yesterday, For it passeth on, yea, a watch by night.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 Thou hast inundated them, they are asleep, In the morning as grass he changeth.
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 In the morning it flourisheth, and hath changed, At evening it is cut down, and hath withered.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 For we were consumed in Thine anger, And in Thy fury we have been troubled.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Thou hast set our iniquities before Thee, Our hidden things at the light of Thy face,
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 For all our days pined away in Thy wrath, We consumed our years as a (meditation)
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 Days of our years, in them [are] seventy years, And if, by reason of might, eighty years, Yet [is] their enlargement labour and vanity, For it hath been cut off hastily, and we fly away.
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Who knoweth the power of Thine anger? And according to Thy fear — Thy wrath?
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 To number our days aright let [us] know, And we bring the heart to wisdom.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Turn back, O Jehovah, till when? And repent concerning Thy servants.
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Satisfy us at morn [with] Thy kindness, And we sing and rejoice all our days.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Cause us to rejoice according to the days Wherein Thou hast afflicted us, The years we have seen evil.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Let Thy work appear unto Thy servants, And Thine honour on their sons.
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 And let the pleasantness of Jehovah our God be upon us, And the work of our hands establish on us, Yea, the work of our hands establish it!
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.