< Psalms 80 >
1 To the Overseer. — 'On the Lilies.' A testimony of Asaph. — A Psalm. Shepherd of Israel, give ear, Leading Joseph as a flock, Inhabiting the cherubs — shine forth,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu. Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli, Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa; Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
2 Before Ephraim, and Benjamin, and Manasseh, Wake up Thy might, and come for our salvation.
kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase. Utsani mphamvu yanu; bwerani ndi kutipulumutsa.
3 O God, cause us to turn back, And cause Thy face to shine, and we are saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu; nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
4 Jehovah, God of Hosts, till when? Thou hast burned against the prayer of Thy people.
Inu Mulungu Wamphamvuzonse, mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
5 Thou hast caused them to eat bread of tears, And causest them to drink With tears a third time.
Mwawadyetsa buledi wa misozi; mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
6 Thou makest us a strife to our neighbours, And our enemies mock at it.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu, ndipo adani athu akutinyoza.
7 God of Hosts, turn us back, And cause Thy face to shine, and we are saved.
Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse, nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.
8 A vine out of Egypt Thou dost bring, Thou dost cast out nations, and plantest it.
Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto; munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
9 Thou hast looked before it, and dost root it, And it filleth the land,
Munawulimira munda wamphesawo, ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 Covered have been hills [with] its shadow, And its boughs [are] cedars of God.
Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake, mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 It sendeth forth its branches unto the sea, And unto the river its sucklings.
Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja, mphukira zake mpaka ku mtsinje.
12 Why hast Thou broken down its hedges, And all passing by the way have plucked it?
Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 A boar out of the forest doth waste it, And a wild beast of the fields consumeth it.
Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 God of Hosts, turn back, we beseech Thee, Look from heaven, and see, and inspect this vine,
Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse! Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone! Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15 And the root that Thy right hand planted, And the branch Thou madest strong for Thee,
muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala, mwana amene inu munamukuza nokha.
16 Burnt with fire — cut down, From the rebuke of Thy face they perish.
Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto; pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Let Thy hand be on the man of Thy right hand, On the son of man Thou hast strengthened for Thyself.
Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja, mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 And we do not go back from Thee, Thou dost revive us, and in Thy name we call.
Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu; titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.
19 O Jehovah, God of Hosts, turn us back, Cause Thy face to shine, and we are saved!
Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse nkhope yanu itiwalire kuti tipulumutsidwe.