< Psalms 51 >

1 To the Overseer. — A Psalm of David, in the coming in unto him of Nathan the prophet, when he hath gone in unto Bath-Sheba. Favour me, O God, according to Thy kindness, According to the abundance of Thy mercies, Blot out my transgressions.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
2 Thoroughly wash me from mine iniquity, And from my sin cleanse me,
Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
3 For my transgressions I do know, And my sin [is] before me continually.
Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
4 Against Thee, Thee only, I have sinned, And done the evil thing in Thine eyes, So that Thou art righteous in Thy words, Thou art pure in Thy judging.
Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
5 Lo, in iniquity I have been brought forth, And in sin doth my mother conceive me.
Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
6 Lo, truth Thou hast desired in the inward parts, And in the hidden part Wisdom Thou causest me to know.
Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
7 Thou cleansest me with hyssop and I am clean, Washest me, and than snow I am whiter.
Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
8 Thou causest me to hear joy and gladness, Thou makest joyful bones Thou hast bruised.
Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
9 Hide Thy face from my sin. And all mine iniquities blot out.
Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
10 A clean heart prepare for me, O God, And a right spirit renew within me.
Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Cast me not forth from Thy presence, And Thy Holy Spirit take not from me.
Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Restore to me the joy of Thy salvation, And a willing spirit doth sustain me.
Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
13 I teach transgressors Thy ways, And sinners unto Thee do return.
Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 Deliver me from blood, O God, God of my salvation, My tongue singeth of Thy righteousness.
Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 O Lord, my lips thou dost open, And my mouth declareth Thy praise.
Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 For Thou desirest not sacrifice, or I give [it], Burnt-offering Thou acceptest not.
Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 The sacrifices of God [are] a broken spirit, A heart broken and bruised, O God, Thou dost not despise.
Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
18 Do good in Thy good pleasure with Zion, Thou dost build the walls of Jerusalem.
Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
19 Then Thou desirest sacrifices of righteousness, Burnt-offering, and whole burnt-offering, Then they offer bullocks on thine altar!
Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

< Psalms 51 >