< Psalms 32 >

1 By David. — An Instruction. O the happiness of him whose transgression [is] forgiven, Whose sin is covered.
Salimo la Davide. Malangizo. Ngodala munthu amene zolakwa zake zakhululukidwa; amene machimo ake aphimbidwa.
2 O the happiness of a man, To whom Jehovah imputeth not iniquity, And in whose spirit there is no deceit.
Ngodala munthu amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3 When I have kept silence, become old have my bones, Through my roaring all the day.
Pamene ndinali chete, mafupa anga anakalamba chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4 When by day and by night Thy hand is heavy upon me, My moisture hath been changed Into the droughts of summer. (Selah)
Pakuti usana ndi usiku dzanja lanu linandipsinja; mphamvu zanga zinatha monga nthawi yotentha yachilimwe. (Sela)
5 My sin I cause Thee to know, And mine iniquity I have not covered. I have said, 'I confess concerning My transgressions to Jehovah,' And Thou — Thou hast taken away, The iniquity of my sin. (Selah)
Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu, sindinabise mphulupulu zanga. Ndinati, “Ine ndidzawulula zolakwa zanga kwa Yehova, ndipo Inu munandikhululukira mlandu wa machimo anga.” (Sela)
6 For this doth every saintly one pray to Thee, As the time to find. Surely at an overflowing of many waters, Unto him they come not.
Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo pomwe mukupezeka; ndithu pamene madzi amphamvu auka, sadzamupeza.
7 Thou [art] a hiding-place for me, From distress Thou dost keep me, [With] songs of deliverance dost compass me. (Selah)
Inu ndi malo anga obisala; muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga ndi nyimbo zachipulumutso. (Sela)
8 I cause thee to act wisely, And direct thee in the way that thou goest, I cause mine eye to take counsel concerning thee.
Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo; ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9 Be ye not as a horse — as a mule, Without understanding, With bridle and bit, its ornaments, to curb, Not to come near unto thee.
Usakhale ngati kavalo kapena bulu, zimene zilibe nzeru, koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu, ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10 Many [are] the pains of the wicked; As to him who is trusting in Jehovah, Kindness doth compass him.
Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa koma chikondi chosatha cha Yehova chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11 Be glad in Jehovah, and rejoice, ye righteous, And sing, all ye upright of heart!
Kondwerani mwa Yehova inu olungama; imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!

< Psalms 32 >