< Psalms 140 >

1 To the Overseer. — A Psalm of David. Deliver me, O Jehovah, from an evil man, From one of violence Thou keepest me.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
2 Who have devised evils in the heart, All the day they assemble [for] wars.
amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
3 They sharpened their tongue as a serpent, Poison of an adder [is] under their lips. (Selah)
Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
4 Preserve me, Jehovah, from the hands of the wicked, From one of violence Thou keepest me, Who have devised to overthrow my steps.
Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
5 The proud hid a snare for me — and cords, They spread a net by the side of the path, Snares they have set for me. (Selah)
Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
6 I have said to Jehovah, 'My God [art] Thou, Hear, Jehovah, the voice of my supplications.'
Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
7 O Jehovah, my Lord, strength of my salvation, Thou hast covered my head in the day of armour.
Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
8 Grant not, O Jehovah, the desires of the wicked, His wicked device bring not forth, They are high. (Selah)
Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
9 The chief of my surrounders, The perverseness of their lips covereth them.
Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
10 They cause to fall on themselves burning coals, Into fire He doth cast them, Into deep pits — they arise not.
Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
11 A talkative man is not established in the earth, One of violence — evil hunteth to overflowing.
Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
12 I have known that Jehovah doth execute The judgment of the afflicted, The judgment of the needy.
Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
13 Only — the righteous give thanks to Thy name, The upright do dwell with Thy presence!
Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.

< Psalms 140 >