< Psalms 124 >

1 A Song of the Ascents, by David. Save [for] Jehovah — who hath been for us, (Pray, let Israel say),
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, anene tsono Israeli,
2 Save [for] Jehovah — who hath been for us, In the rising up of man against us,
akanapanda kukhala mbali yathu Yehova, potiwukira anthuwo,
3 Then alive they had swallowed us up, In the burning of their anger against us,
iwo atatipsera mtima, akanatimeza amoyo;
4 Then the waters had overflowed us, The stream passed over our soul,
chigumula chikanatimiza, mtsinje ukanatikokolola,
5 Then passed over our soul had the proud waters.
madzi a mkokomo akanatikokolola.
6 Blessed [is] Jehovah who hath not given us, A prey to their teeth.
Atamandike Yehova, amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7 Our soul as a bird hath escaped from a snare of fowlers, The snare was broken, and we have escaped.
Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame yokodwa mu msampha wa mlenje; msampha wathyoka, ndipo ife tapulumuka.
8 Our help [is] in the name of Jehovah, Maker of the heavens and earth!
Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

< Psalms 124 >