< Psalms 118 >

1 Give ye thanks to Jehovah, For good, for to the age [is] His kindness.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 I pray you, let Israel say, That, to the age [is] His kindness.
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 I pray you, let the house of Aaron say, That, to the age [is] His kindness.
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 I pray you, let those fearing Jehovah say, That, to the age [is] His kindness.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 From the straitness I called Jah, Jah answered me in a broad place.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Jehovah [is] for me, I do not fear what man doth to me.
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Jehovah [is] for me among my helpers, And I — I look on those hating me.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Better to take refuge in Jehovah than to trust in man,
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Better to take refuge in Jehovah, Than to trust in princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 All nations have compassed me about, In the name of Jehovah I surely cut them off.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 They have compassed me about, Yea, they have compassed me about, In the name of Jehovah I surely cut them off.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 They compassed me about as bees, They have been extinguished as a fire of thorns, In the name of Jehovah I surely cut them off.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Thou hast sorely thrust me to fall, And Jehovah hath helped me.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 My strength and song [is] Jah, And He is to me for salvation.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 A voice of singing and salvation, [Is] in the tents of the righteous, The right hand of Jehovah is doing valiantly.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 The right hand of Jehovah is exalted, The right hand of Jehovah is doing valiantly.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 I do not die, but live, And recount the works of Jah,
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Jah hath sorely chastened me, And to death hath not given me up.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Open ye to me gates of righteousness, I enter into them — I thank Jah.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 This [is] the gate to Jehovah, The righteous enter into it.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 I thank Thee, for Thou hast answered me, And art to me for salvation.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 A stone the builders refused Hath become head of a corner.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 From Jehovah hath this been, It [is] wonderful in our eyes,
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 This [is] the day Jehovah hath made, We rejoice and are glad in it.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 I beseech Thee, O Jehovah, save, I pray Thee, I beseech Thee, O Jehovah, prosper, I pray Thee.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Blessed [is] he who is coming In the name of Jehovah, We blessed you from the house of Jehovah,
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 God [is] Jehovah, and He giveth to us light, Direct ye the festal-sacrifice with cords, Unto the horns of the altar.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 My God Thou [art], and I confess Thee, My God, I exalt Thee.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Give ye thanks to Jehovah, For good, for to the age, [is] His kindness!
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalms 118 >