< Psalms 11 >

1 To the Overseer. — By David. In Jehovah I trusted, how say ye to my soul, 'They moved [to] Thy mountain for the bird?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
2 For lo, the wicked tread a bow, They have prepared their arrow on the string, To shoot in darkness at the upright in heart.
Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
3 When the foundations are destroyed, The righteous — what hath he done?
Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
4 'Jehovah [is] in his holy temple: Jehovah — in the heavens [is] His throne. His eyes see — His eyelids try the sons of men.
Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
5 Jehovah the righteous doth try. And the wicked and the lover of violence, Hath His soul hated,
Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
6 He poureth on the wicked snares, fire, and brimstone, And a horrible wind [is] the portion of their cup.
Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
7 For righteous [is] Jehovah, Righteousness He hath loved, The upright doth His countenance see!'
Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.

< Psalms 11 >