< Proverbs 7 >
1 My son! keep my sayings, And my commands lay up with thee.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Keep my commands, and live, And my law as the pupil of thine eye.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Bind them on thy fingers, Write them on the tablet of thy heart.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Say to wisdom, 'My sister Thou [art].' And cry to understanding, 'Kinswoman!'
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 To preserve thee from a strange woman, From a stranger who hath made smooth her sayings.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 For, at a window of my house, Through my casement I have looked out,
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 And I do see among the simple ones, I discern among the sons, A young man lacking understanding,
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Passing on in the street, near her corner, And the way [to] her house he doth step,
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 In the twilight — in the evening of day, In the darkness of night and blackness.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 And, lo, a woman to meet him — (A harlot's dress, and watchful of heart,
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 Noisy she [is], and stubborn, In her house her feet rest not.
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Now in an out-place, now in broad places, And near every corner she lieth in wait) —
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 And she laid hold on him, and kissed him, She hath hardened her face, and saith to him,
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 'Sacrifices of peace-offerings [are] by me, To-day I have completed my vows.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 Therefore I have come forth to meet thee, To seek earnestly thy face, and I find thee.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 [With] ornamental coverings I decked my couch, Carved works — cotton of Egypt.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 I sprinkled my bed — myrrh, aloes, and cinnamon.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Come, we are filled [with] loves till the morning, We delight ourselves in loves.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 For the man is not in his house, He hath gone on a long journey.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 A bag of money he hath taken in his hand, At the day of the new moon he cometh to his house.'
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 She turneth him aside with the abundance of her speech, With the flattery of her lips she forceth him.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 He is going after her straightway, As an ox unto the slaughter he cometh, And as a fetter unto the chastisement of a fool,
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 Till an arrow doth split his liver, As a bird hath hastened unto a snare, And hath not known that it [is] for its life.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 And now, ye sons, hearken to me, And give attention to sayings of my mouth.
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Let not thy heart turn unto her ways, Do not wander in her paths,
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 For many [are] the wounded she caused to fall, And mighty [are] all her slain ones.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 The ways of Sheol — her house, Going down unto inner chambers of death! (Sheol )
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )