< Proverbs 28 >

1 The wicked have fled and there is no pursuer. And the righteous as a young lion is confident.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 By the transgression of a land many [are] its heads. And by an intelligent man, Who knoweth right — it is prolonged.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 A man — poor and oppressing the weak, [Is] a sweeping rain, and there is no bread.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Those forsaking the law praise the wicked, Those keeping the law plead against them.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Evil men understand not judgment, And those seeking Jehovah understand all.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Better [is] the poor walking in his integrity, Than the perverse of ways who is rich.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Whoso is keeping the law is an intelligent son, And a friend of gluttons, Doth cause his father to blush.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 Whoso is multiplying his wealth by biting and usury, For one favouring the poor doth gather it.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Whoso is turning his ear from hearing the law, Even his prayer [is] an abomination.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Whoso is causing the upright to err in an evil way, Into his own pit he doth fall, And the perfect do inherit good.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 A rich man is wise in his own eyes, And the intelligent poor searcheth him.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 In the exulting of the righteous the glory [is] abundant, And in the rising of the wicked man is apprehensive.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 Whoso is covering his transgressions prospereth not, And he who is confessing and forsaking hath mercy.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 O the happiness of a man fearing continually, And whoso is hardening his heart falleth into evil.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 A growling lion, and a ranging bear, [Is] the wicked ruler over a poor people.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 A leader lacking understanding multiplieth oppressions, Whoso is hating dishonest gain prolongeth days.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 A man oppressed with the blood of a soul, Unto the pit fleeth, none taketh hold on him.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Whoso is walking uprightly is saved, And the perverted of ways falleth at once.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Whoso is tilling his ground is satisfied [with] bread, And whoso is pursuing vanity, Is filled [with] poverty.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 A stedfast man hath multiplied blessings, And whoso is hasting to be rich is not acquitted.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 To discern faces is not good, And for a piece of bread doth a man transgress.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 Troubled for wealth [is] the man [with] an evil eye, And he knoweth not that want doth meet him.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Whoso is reproving a man afterwards findeth grace, More than a flatterer with the tongue.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Whoso is robbing his father, or his mother, And is saying, 'It is not transgression,' A companion he is to a destroyer.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Whoso is proud in soul stirreth up contention, And whoso is trusting on Jehovah is made fat.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Whoso is trusting in his heart is a fool, And whoso is walking in wisdom is delivered.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Whoso is giving to the poor hath no lack, And whoso is hiding his eyes multiplied curses.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 In the rising of the wicked a man is hidden, And in their destruction the righteous multiply!
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Proverbs 28 >