< Proverbs 16 >
1 Of man [are] arrangements of the heart, And from Jehovah an answer of the tongue.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 All the ways of a man are pure in his own eyes, And Jehovah is pondering the spirits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Roll unto Jehovah thy works, And established are thy purposes,
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 All things hath Jehovah wrought for Himself, And also the wicked [worketh] for a day of evil.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 An abomination to Jehovah [is] every proud one of heart, Hand to hand he is not acquitted.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 In kindness and truth pardoned is iniquity, And in the fear of Jehovah Turn thou aside from evil.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 When a man's ways please Jehovah, even his enemies, He causeth to be at peace with him.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Better [is] a little with righteousness, Than abundance of increase without justice.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 The heart of man deviseth his way, And Jehovah establisheth his step.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 An oath [is] on the lips of a king, In judgment his mouth trespasseth not.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 A just beam and balances [are] Jehovah's, His work [are] all the stones of the bag.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 An abomination to kings [is] doing wickedness, For by righteousness is a throne established.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 The delight of kings [are] righteous lips, And whoso is speaking uprightly he loveth,
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 The fury of a king [is] messengers of death, And a wise man pacifieth it.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 In the light of a king's face [is] life, And his good-will [is] as a cloud of the latter rain.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 To get wisdom — how much better than gold, And to get understanding to be chosen than silver!
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 A highway of the upright [is], 'Turn from evil,' Whoso is preserving his soul is watching his way.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 Before destruction [is] pride, And before stumbling — a haughty spirit.'
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Better is humility of spirit with the poor, Than to apportion spoil with the proud.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 The wise in any matter findeth good, And whoso is trusting in Jehovah, O his happiness.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 To the wise in heart is called, 'Intelligent,' And sweetness of lips increaseth learning.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 A fountain of life [is] understanding to its possessors, The instruction of fools is folly.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 The heart of the wise causeth his mouth to act wisely, And by his lips he increaseth learning,
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Sayings of pleasantness [are] a honeycomb, Sweet to the soul, and healing to the bone.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 There is a way right before a man, And its latter end — ways of death.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 A labouring man hath laboured for himself, For his mouth hath caused [him] to bend over it.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 A worthless man is preparing evil, And on his lips — as a burning fire.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 A froward man sendeth forth contention, A tale-bearer is separating a familiar friend.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 A violent man enticeth his neighbour, And hath causeth him to go in a way not good.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Consulting his eyes to devise froward things, Moving his lips he hath accomplished evil.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 A crown of beauty [are] grey hairs, In the way of righteousness it is found.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Better [is] the slow to anger than the mighty, And the ruler over his spirit than he who is taking a city.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Into the centre is the lot cast, And from Jehovah [is] all its judgment!
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.