< Proverbs 10 >
1 Proverbs of Solomon. A wise son causeth a father to rejoice, And a foolish son [is] an affliction to his mother.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Treasures of wickedness profit not, And righteousness delivereth from death.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 Jehovah causeth not the soul of the righteous to hunger, And the desire of the wicked He thrusteth away.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Poor [is] he who is working — a slothful hand, And the hand of the diligent maketh rich.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 Whoso is gathering in summer [is] a wise son, Whoso is sleeping in harvest [is] a son causing shame.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Blessings [are] for the head of the righteous, And the mouth of the wicked cover doth violence.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 The remembrance of the righteous [is] for a blessing, And the name of the wicked doth rot.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 The wise in heart accepteth commands, And a talkative fool kicketh.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Whoso is walking in integrity walketh confidently, And whoso is perverting his ways is known.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Whoso is winking the eye giveth grief, And a talkative fool kicketh.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 A fountain of life [is] the mouth of the righteous, And the mouth of the wicked cover doth violence.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Hatred awaketh contentions, And over all transgressions love covereth.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 In the lips of the intelligent is wisdom found, And a rod [is] for the back of him who is lacking understanding.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 The wise lay up knowledge, and the mouth of a fool [is] near ruin.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 The wealth of the rich [is] his strong city, The ruin of the poor [is] their poverty.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 The wage of the righteous [is] for life, The increase of the wicked for sin.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 A traveller to life [is] he who is keeping instruction, And whoso is forsaking rebuke is erring.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Whoso is covering hatred with lying lips, And whoso is bringing out an evil report is a fool.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 In the abundance of words transgression ceaseth not, And whoso is restraining his lips [is] wise.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 The tongue of the righteous [is] chosen silver, The heart of the wicked — as a little thing.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 The lips of the righteous delight many, And fools for lack of heart die.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 The blessing of Jehovah — it maketh rich, And He addeth no grief with it.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 To execute inventions [is] as play to a fool, And wisdom to a man of understanding.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 The feared thing of the wicked it meeteth him, And the desire of the righteous is given.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 As the passing by of a hurricane, So the wicked is not, And the righteous is a foundation age-during.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 As vinegar to the teeth, And as smoke to the eyes, So [is] the slothful to those sending him.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 The fear of Jehovah addeth days, And the years of the wicked are shortened.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 The hope of the righteous [is] joyful, And the expectation of the wicked perisheth.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 The way of Jehovah [is] strength to the perfect, And ruin to workers of iniquity.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 The righteous to the age is not moved, And the wicked inhabit not the earth.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 The mouth of the righteous uttereth wisdom, And the tongue of frowardness is cut out.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 The lips of the righteous know a pleasing thing, And the mouth of the wicked perverseness!
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.