< Numbers 34 >
1 And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 'Command the sons of Israel, and thou hast said unto them, When ye are coming in unto the land of Canaan — this [is] the land which falleth to you by inheritance, the land of Canaan, by its borders —
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 then hath the south quarter been to you from the wilderness of Zin, by the sides of Edom, yea, the south border hath been to you from the extremity of the Salt Sea, eastward;
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 and the border hath turned round to you from the south to the ascent of Akrabbim, and hath passed on to Zin, and its outgoings have been from the south to Kadesh-Barnea, and it hath gone out at Hazar-Addar, and hath passed on to Azmon;
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 and the border hath turned round from Azmon to the brook of Egypt, and its outgoings have been at the sea.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 'As to the west border, even the great sea hath been to you a border; this is to you the west border.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 'And this is to you the north border: from the great sea ye mark out for yourselves mount Hor;
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 from mount Hor ye mark out to go in to Hamath, and the outgoings of the border have been to Zedad;
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 and the border hath gone out to Ziphron, and its outgoings have been at Hazar-Enan; this is to you the north border.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 'And ye have marked out for yourselves for the border eastward, from Hazar-Enan to Shepham;
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 and the border hath gone down from Shepham to Riblah, on the east of Ain, and the border hath gone down, and hath smitten against the shoulder of the sea of Chinnereth eastward;
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 and the border hath gone down to the Jordan, and its outgoings have been at the Salt Sea; this is for you the land by its borders round about.'
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 And Moses commandeth the sons of Israel, saying, 'This [is] the land which ye inherit by lot, which Jehovah hath commanded to give to the nine tribes and the half of the tribe;
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 for the tribe of the sons of Reuben have received, by the house of their fathers; and the tribe of the children of Gad, by the house of their fathers; and the half of the tribe of Manasseh have received their inheritance;
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 the two tribes and the half of the tribe have received their inheritance beyond the Jordan, [near] Jericho, eastward, at the [sun] -rising.'
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 'These [are] the names of the men who give to you the inheritance of the land: Eleazar the priest, and Joshua son of Nun,
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 and one prince — one prince — for a tribe ye do take to give the land by inheritance.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 'And these [are] the names of the men: of the tribe of Judah, Caleb son of Jephunneh;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 and of the tribe of the sons of Simeon, Shemuel son of Aminihud;
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 of the tribe of Benjamin, Elidad son of Chislon;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 and of the tribe of the sons of Dan, the prince Bukki son of Jogli;
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 of the sons of Joseph, of the tribe of the sons of Manasseh, the prince Hanniel son of Ephod;
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 and of the tribe of the sons of Ephraim, the prince Kemuel son of Shiphtan;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 and of the tribe of the sons of Zebulun, the prince Elizaphan son of Parnach;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 and of the tribe of the sons of Issachar, the prince Paltiel son of Azzan;
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 and of the tribe of the sons of Asher, the prince Ahihud son of Shelomi;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 and of the tribe of the sons of Naphtali, the prince Pedahel son of Ammihud.'
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 These [are] those whom Jehovah hath commanded to give the sons of Israel inheritance in the land of Canaan.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.