< Numbers 17 >
1 And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 'Speak unto the sons of Israel, and take from them each a rod, for a father's house, from all their princes, for the house of their fathers, twelve rods; the name of each thou dost write on his rod,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
3 and Aaron's name thou dost write on the tribe of Levi; for one rod [is] for the head of their fathers' house:
Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
4 and thou hast placed them in the tent of meeting, before the testimony, where I meet with you.
Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
5 'And it hath come to pass, the man's rod on whom I fix doth flourish, and I have caused to cease from off me the murmurings of the sons of Israel, which they are murmuring against you.'
Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
6 And Moses speaketh unto the sons of Israel, and all their princes give unto him one rod for a prince, one rod for a prince, for their fathers' house, twelve rods, and the rod of Aaron [is] in the midst of their rods;
Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
7 and Moses placeth the rods before Jehovah, in the tent of the testimony.
Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
8 And it cometh to pass, on the morrow, that Moses goeth in unto the tent of the testimony, and lo, the rod of Aaron hath flourished for the house of Levi, and is bringing out flourishing, and doth blossom blossoms, and doth produce almonds;
Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
9 and Moses bringeth out all the rods from before Jehovah, unto all the sons of Israel, and they look, and take each his rod.
Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
10 And Jehovah saith unto Moses, 'Put back the rod of Aaron, before the testimony, for a charge, for a sign to the sons of rebellion, and thou dost remove their murmurings from off me, and they do not die;'
Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
11 and Moses doth as Jehovah hath commanded him; so he hath done.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
12 And the sons of Israel speak unto Moses, saying, 'Lo, we have expired; we have perished; we have all of us perished;
Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
13 any who is at all drawing near unto the tabernacle of Jehovah dieth; have we not been consumed — to expire?'
Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”