< Nehemiah 6 >
1 And it cometh to pass, when it hath been heard by Sanballat, and Tobiah, and by Geshem the Arabian, and by the rest of our enemies, that I have builded the wall, and there hath not been left in it a breach, (also, till that time the doors I had not set up in the gates, )
Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
2 that Sanballat sendeth, also Geshem, unto me, saying, 'Come and we meet together in the villages, in the valley of Ono;' and they are thinking to do to me evil.
Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
3 And I send unto them messengers, saying, 'A great work I am doing, and I am not able to come down; why doth the work cease when I let it alone, and have come down unto you?'
Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
4 and they send unto me, according to this word, four times, and I return them [word] according to this word.
Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
5 And Sanballat sendeth unto me, according to this word, a fifth time, his servant, and an open letter in his hand;
Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
6 it is written in it, 'Among the nations it hath been heard, and Gashmu is saying: Thou and the Jews are thinking to rebel, therefore thou art building the wall, and thou hast been to them for a king — according to these words!
Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
7 And also, prophets thou hast appointed to call for thee in Jerusalem, saying, A king [is] in Judah, and now it is heard by the king according to these words; and now come, and we take counsel together.'
Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
8 And I send unto him, saying, 'It hath not been according to these words that thou art saying, for from thine own heart thou art devising them;'
Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
9 for all of them are making us afraid, saying, 'Their hands are too feeble for the work, and it is not done;' and now, strengthen Thou my hands.
Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
10 And I have entered the house of Shemaiah son of Delaiah, son of Mehetabeel — and he is restrained — and he saith, 'Let us meet at the house of God, at the inside of the temple, and we shut the doors of the temple, for they are coming in to slay thee — yea, by night they are coming in to slay thee.'
Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
11 And I say, 'A man such as I — doth he flee? and who as I, that doth go in unto the temple, and live? — I do not go in.'
Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
12 And I discern, and lo, God hath not sent him, for in the prophecy he hath spoken unto me both Tobiah and Sanballat hired him,
Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
13 so that he [is] an hireling, that I may fear and do so, and I had sinned, and it had been to them for an evil name that they may reproach me.
Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
14 Be mindful, O my God, of Tobiah, and of Sanballat, according to these his works, and also, of Noadiah the prophetess, and of the rest of the prophets who have been making me afraid.
Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
15 And the wall is completed in the twenty and fifth of Elul, on the fifty and second day;
Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
16 and it cometh to pass, when all our enemies have heard, and all the nations who are round about us see, that they fall greatly in their own eyes, and know that by our God hath this work been done.
Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
17 Also, in those days the freemen of Judah are multiplying their letters going unto Tobiah, and those of Tobiah are coming in unto them;
Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
18 for many in Judah are sworn to him, for he [is] son-in-law to Shechaniah son of Arah, and Jehohanan his son hath taken the daughter of Meshullam son of Berechiah;
pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
19 also, his good deeds they have been saying before me, and my words they have been taking out to him; letters hath Tobiah sent to make me afraid.
Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.