< Leviticus 25 >

1 And Jehovah speaketh unto Moses, in mount Sinai, saying,
Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
2 'Speak unto the sons of Israel, and thou hast said unto them, When ye come in unto the land which I am giving to you, then hath the land kept a sabbath to Jehovah.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
3 'Six years thou dost sow thy field, and six years thou dost prune thy vineyard, and hast gathered its increase,
Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
4 and in the seventh year a sabbath of rest is to the land, a sabbath to Jehovah; thy field thou dost not sow, and thy vineyard thou dost not prune;
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
5 the spontaneous growth of thy harvest thou dost not reap, and the grapes of thy separated thing thou dost not gather, a year of rest it is to the land.
Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
6 'And the sabbath of the land hath been to you for food, to thee, and to thy man-servant, and to thy handmaid, and to thy hireling, and to thy settler, who are sojourning with thee;
Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
7 and to thy cattle, and to the beast which [is] in thy land, is all thine increase for food.
Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
8 'And thou hast numbered to thee seven sabbaths of years, seven years seven times, and the days of the seven sabbaths of years have been to thee nine and forty years,
“‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
9 and thou hast caused a trumpet of shouting to pass over in the seventh month, in the tenth of the month; in the day of the atonements ye do cause a trumpet to pass over through all your land;
Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
10 and ye have hallowed the year, the fiftieth year; and ye have proclaimed liberty in the land to all its inhabitants; a jubilee it is to you; and ye have turned back each unto his possession; yea, each unto his family ye do turn back.
Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
11 'A jubilee it [is], the fiftieth year, a year it is to you; ye sow not, nor reap its spontaneous growth, nor gather its separated things;
Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
12 for a jubilee it [is], holy it is to you; out of the field ye eat its increase;
Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
13 in the year of this jubilee ye turn back each unto his possession.
“‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
14 'And when thou sellest anything to thy fellow, or buyest from the hand of thy fellow, ye do not oppress one another;
“‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
15 by the number of years after the jubilee thou dost buy from thy fellow; by the number of the years of increase he doth sell to thee;
Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
16 according to the multitude of the years thou dost multiply its price, and according to the fewness of the years thou dost diminish its price; for a number of increases he is selling to thee;
Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
17 and ye do not oppress one another, and thou hast been afraid of thy God; for I [am] Jehovah your God.
Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
18 'And ye have done My statutes, and My judgments ye keep, and have done them, and ye have dwelt on the land confidently,
“‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
19 and the land hath given its fruit, and ye have eaten to satiety, and have dwelt confidently on it.
Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
20 'And when ye say, What do we eat in the seventh year, lo, we do not sow, nor gather our increase?
Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
21 then I have commanded My blessing on you in the sixth year, and it hath made the increase for three years;
Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
22 and ye have sown the eighth year, and have eaten of the old increase; until the ninth year, until the coming in of its increase, ye do eat the old.
Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
23 'And the land is not sold — to extinction, for the land [is] Mine, for sojourners and settlers [are] ye with Me;
“‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
24 and in all the land of your possession a redemption ye do give to the land.
Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
25 'When thy brother becometh poor, and hath sold his possession, then hath his redeemer who is near unto him come, and he hath redeemed the sold thing of his brother;
“‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
26 and when a man hath no redeemer, and his own hand hath attained, and he hath found as sufficient [for] its redemption,
Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
27 then he hath reckoned the years of its sale, and hath given back that which is over to the man to whom he sold [it], and he hath returned to his possession.
Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
28 'And if his hand hath not found sufficiency to give back to him, then hath his sold thing been in the hand of him who buyeth it till the year of jubilee; and it hath gone out in the jubilee, and he hath returned to his possession.
Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
29 'And when a man selleth a dwelling-house [in] a walled city, then hath his right of redemption been until the completion of a year from its selling; days — is his right of redemption;
“‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
30 and if it is not redeemed until the fulness to him of a perfect year, then hath the house which [is] in a walled city been established to extinction to the buyer of it, to his generations; it goeth not out in the jubilee;
Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
31 and a house of the villages which have no wall round about, on the field of the country is reckoned; redemption is to it, and in the jubilee it goeth out.
Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
32 'As to cities of the Levites — houses of the cities of their possession — redemption age-during is to the Levites;
“‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
33 as to him who redeemeth from the Levites, both the sale of a house and the city of his possession have gone out in the jubilee, for the houses of the cities of the Levites are their possession in the midst of the sons of Israel.
Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
34 And a field, a suburb of their cities, is not sold; for a possession age-during it [is] to them.
Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
35 'And when thy brother is become poor, and his hand hath failed with thee, then thou hast kept hold on him, sojourner and settler, and he hath lived with thee;
“‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
36 thou takest no usury from him, or increase; and thou hast been afraid of thy God; and thy brother hath lived with thee;
Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
37 thy money thou givest not to him in usury, and for increase thou givest not thy food;
Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
38 I [am] Jehovah your God, who hath brought you out of the land of Egypt, to give to you the land of Canaan, to become your God.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
39 'And when thy brother becometh poor with thee, and he hath been sold to thee, thou dost not lay on him servile service;
“‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
40 as an hireling, as a settler, he is with thee, till the year of the jubilee he doth serve with thee, —
Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
41 then he hath gone out from thee, he and his sons with him, and hath turned back unto his family; even unto the possession of his fathers he doth turn back.
Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
42 'For they [are] My servants, whom I have brought out from the land of Egypt: they are not sold [with] the sale of a servant;
Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
43 thou rulest not over him with rigour, and thou hast been afraid of thy God.
Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
44 'And thy man-servant and thy handmaid whom thou hast [are] of the nations who [are] round about you; of them ye buy man-servant and handmaid,
“‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
45 and also of the sons of the settlers who are sojourning with you, of them ye buy, and of their families who [are] with you, which they have begotten in your land, and they have been to you for a possession;
Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
46 and ye have taken them for inheritance to your sons after you, to occupy [for] a possession; to the age ye lay service upon them, but upon your brethren, the sons of Israel, one with another, thou dost not rule over him with rigour.
Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
47 'And when the hand of a sojourner or settler with thee attaineth [riches], and thy brother with him hath become poor, and he hath been sold to a sojourner, a settler with thee, or to the root of the family of a sojourner,
“‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
48 after he hath been sold, there is a right of redemption to him; one of his brethren doth redeem him,
wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
49 or his uncle, or a son of his uncle, doth redeem him, or any of the relations of his flesh, of his family, doth redeem him, or — his own hand hath attained — then he hath been redeemed.
amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
50 'And he hath reckoned with his buyer from the year of his being sold to him till the year of jubilee, and the money of his sale hath been by the number of years; as the days of an hireling it is with him.
Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
51 'If yet many years, according to them he giveth back his redemption [money], from the money of his purchase.
Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
52 'And if few are left of the years till the year of jubilee, then he hath reckoned with him, according to his years he doth give back his redemption [money];
Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
53 as an hireling, year by year, he is with him, and he doth not rule him with rigour before thine eyes.
Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
54 'And if he is not redeemed in these [years], then he hath gone out in the year of jubilee, he and his sons with him.
“‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
55 For to Me [are] the sons of Israel servants; My servants they [are], whom I have brought out of the land of Egypt; I, Jehovah, [am] your God.
pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

< Leviticus 25 >