< Leviticus 21 >

1 And Jehovah saith unto Moses, 'Speak unto the priests, sons of Aaron, and thou hast said unto them, For [any] person [a priest] is not defiled among his people,
Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
2 except for his relation who [is] near unto him — for his mother, and for his father, and for his son, and for his daughter, and for his brother.
Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
3 and for his sister, the virgin, who is near unto him, who hath not been to a man; for her he is defiled.
kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
4 'A master [priest] doth not defile himself among his people — to pollute himself;
Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
5 they do not make baldness on their head, and the corner of their beard they do not shave, and in their flesh they do not make a cutting;
“‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
6 they are holy to their God, and they pollute not the name of their God, for the fire-offerings of Jehovah, bread of their God, they are bringing near, and have been holy.
Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
7 'A woman, a harlot, or polluted, they do not take, and a woman cast out from her husband they do not take, for he [is] holy to his God;
“‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
8 and thou hast sanctified him, for the bread of thy God he is bringing near; he is holy to thee; for holy [am] I, Jehovah, sanctifying you.
Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
9 'And a daughter of any priest when she polluteth herself by going a-whoring — her father she is polluting; with fire she is burnt.
“‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
10 'And the high priest of his brethren, on whose head is poured the anointing oil, and hath consecrated his hand to put on the garments, his head doth not uncover, nor rend his garments,
“‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
11 nor beside any dead person doth he come; for his father and for his mother he doth not defile himself;
Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
12 nor from the sanctuary doth he go out, nor doth he pollute the sanctuary of his God, for the separation of the anointing oil of his God [is] on him; I [am] Jehovah.
Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
13 'And he taketh a wife in her virginity;
“‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
14 widow, or cast out, or polluted one — a harlot — these he doth not take, but a virgin of his own people he doth take [for] a wife,
Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
15 and he doth not pollute his seed among his people; for I [am] Jehovah, sanctifying him.'
kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
16 And Jehovah speaketh unto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 'Speak unto Aaron, saying, No man of thy seed to their generations in whom there is blemish doth draw near to bring near the bread of his God,
“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
18 for no man in whom [is] blemish doth draw near — a man blind, or lame or dwarfed, or enlarged,
Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
19 or a man in whom there is a breach in the foot, or a breach in the hand,
munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
20 or hump-backed, or a dwarf, or with a mixture in his eye, or a scurvy person, or scabbed, or broken-testicled.
kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
21 'No man in whom is blemish (of the seed of Aaron the priest) doth come nigh to bring near the fire-offerings of Jehovah; blemish [is] in him; the bread of his God he doth not come nigh to bring near.
Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
22 'Bread of his God — of the most holy things, and of the holy things — he doth eat;
Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
23 only, unto the vail he doth not enter, and unto the altar he doth not draw nigh; for blemish [is] in him; and he doth not pollute My sanctuaries; for I [am] Jehovah, sanctifying them.'
Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
24 And Moses speaketh unto Aaron, and unto his sons, and unto all the sons of Israel.
Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.

< Leviticus 21 >