< Joshua 8 >

1 And Jehovah saith unto Joshua, 'Fear not, nor be affrighted, take with thee all the people of war, and rise, go up to Ai; see, I have given into thy hand the king of Ai, and his people, and his city, and his land,
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
2 and thou hast done to Ai and to her king as thou hast done to Jericho and to her king; only, its spoil and its cattle ye spoil for yourselves; set for thee an ambush for the city at its rear.'
Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
3 And Joshua riseth, and all the people of war, to go up to Ai, and Joshua chooseth thirty thousand men, mighty ones of valour, and sendeth them away by night,
Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
4 and commandeth them, saying, 'See, ye are liers in wait against the city, at the rear of the city, ye go not very far off from the city, and all of you have been prepared,
nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
5 and I and all the people who [are] with me draw near unto the city, and it hath come to pass when they come out to meet us as at the first, and we have fled before them,
Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
6 and they have come out after us till we have drawn them out of the city, for they say, They are fleeing before us as at the first, and we have fled before them,
Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
7 and ye rise from the ambush, and have occupied the city, and Jehovah your God hath given it into your hand;
inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
8 and it hath been, when ye capture the city, ye burn the city with fire, according to the word of Jehovah ye do, see, I have commanded you.'
Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
9 And Joshua sendeth them away, and they go unto the ambush, and abide between Bethel and Ai, on the west of Ai; and Joshua lodgeth on that night in the midst of the people.
Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
10 And Joshua riseth early in the morning, and inspecteth the people, and goeth up, he and the elders of Israel, before the people to Ai;
Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
11 and all the people of war who [are] with him have gone up, and draw nigh and come in over-against the city, and encamp on the north of Ai; and the valley [is] between him and Ai.
Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
12 And he taketh about five thousand men, and setteth them an ambush between Bethel and Ai, on the west of the city;
Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
13 and they set the people, all the camp which [is] on the north of the city, and its rear on the west of the city, and Joshua goeth on that night into the midst of the valley.
Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
14 And it cometh to pass, when the king of Ai seeth [it], that hasten, and rise early, and go out do the men of the city to meet Israel for battle, he and all his people, at the appointed season, at the front of the plain, and he hath not known that an ambush [is] against him, on the rear of the city.
Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
15 And Joshua and all Israel [seem] stricken before them, and flee the way of the wilderness,
Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
16 and all the people who [are] in the city are called to pursue after them, and they pursue after Joshua, and are drawn away out of the city,
Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
17 and there hath not been left a man in Ai and Bethel who hath not gone out after Israel, and they leave the city open, and pursue after Israel.
Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
18 And Jehovah saith unto Joshua, 'Stretch out with the javelin which [is] in thy hand towards Ai, for into thy hand I give it;' and Joshua stretcheth out with the javelin which [is] in his hand toward the city,
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
19 and the ambush hath risen [with] haste, out of its place, and they run at the stretching out of his hand, and go into the city, and capture it, and hasten, and burn the city with fire.
Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
20 And the men of Ai look behind them, and see, and lo, the smoke of the city hath gone up unto the heavens, and there hath not been in them power to flee hither and thither — and the people who are fleeing to the wilderness have turned against the pursuer, —
Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
21 and Joshua and all Israel have seen that the ambush hath captured the city, and that the smoke of the city hath gone up, and they turn back and smite the men of Ai;
Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
22 and these have come out from the city to meet them, and they are in the midst of Israel, some on this side, and some on that, and they smite them till he hath not left to them a remnant and escaped one;
Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
23 and the king of Ai they caught alive, and bring him near unto Joshua.
kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
24 And it cometh to pass, at Israel's finishing to slay all the inhabitants of Ai in the field, in the wilderness in which they pursued them (and they fall all of them by the mouth of the sword till their consumption), that all Israel turn back to Ai, and smite it by the mouth of the sword;
Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
25 and all who fall during the day, of men and of women, are twelve thousand — all men of Ai.
Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
26 And Joshua hath not brought back his hand which he stretched out with the javelin till that he hath devoted all the inhabitants of Ai;
Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
27 only, the cattle and the spoil of that city have Israel spoiled for themselves, according to the word of Jehovah which He commanded Joshua.
Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
28 And Joshua burneth Ai, and maketh it a heap age-during — a desolation unto this day;
Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
29 and the king of Ai he hath hanged on the tree till even-time, and at the going in of the sun hath Joshua commanded, and they take down his carcase from the tree, and cast it unto the opening of the gate of the city, and raise over it a great heap of stones till this day.
Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
30 Then doth Joshua build an altar to Jehovah, God of Israel, in mount Ebal,
Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
31 as Moses, servant of Jehovah, commanded the sons of Israel, as it is written in the book of the law of Moses — an altar of whole stones, over which he hath not waved iron — and they cause to go up upon it burnt-offerings to Jehovah, and sacrifice peace-offerings;
Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
32 and he writeth there on the stones the copy of the law of Moses, which he hath written in the presence of the sons of Israel.
Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
33 And all Israel, and its elders, and authorities, and its judges, are standing on this side and on that of the ark, over-against the priests, the Levites, bearing the ark of the covenant of Jehovah, as well the sojourner as the native, half of them over-against mount Gerizim, and the half of them over-against mount Ebal, as Moses servant of Jehovah commanded to bless the people of Israel at the first.
Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
34 And afterwards he hath proclaimed all the words of the law, the blessing and the reviling, according to all that is written in the book of the law;
Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
35 there hath not been a thing of all that Moses commanded which Joshua hath not proclaimed before all the assembly of Israel, and the women, and the infants, and the sojourner who is going in their midst.
Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.

< Joshua 8 >