< Joshua 18 >

1 And all the company of the sons of Israel are assembled [at] Shiloh, and they cause the tent of meeting to tabernacle there, and the land hath been subdued before them.
Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
2 And there are left among the sons of Israel who have not shared their inheritance, seven tribes,
Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
3 and Joshua saith unto the sons of Israel, 'Till when are ye remiss to go in to possess the land which He hath given to you, Jehovah, God of your fathers?
Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
4 Give for you three men for a tribe, and I send them, and they rise and go up and down through the land, and describe it according to their inheritance, and come in unto me,
Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
5 and they have divided it into seven portions — Judah doth stay by its border on the south, and the house of Joseph do stay by their border on the north —
Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
6 and ye describe the land [in] seven portions, and have brought [it] in unto me hither, and I have cast for you a lot here before Jehovah our God;
Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
7 for there is no portion to the Levites in your midst, for the priesthood of Jehovah [is] their inheritance, and Gad, and Reuben, and the half of the tribe of Manasseh received their inheritance beyond the Jordan eastward, which Moses servant of Jehovah gave to them.'
Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
8 And the men rise and go; and Joshua commandeth those who are going to describe the land, saying, 'Go, and walk up and down through the land, and describe it, and turn back unto me, and here I cast for you a lot before Jehovah in Shiloh.'
Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
9 And the men go, and pass over through the land, and describe it by cities, in seven portions, on a book, and they come in unto Joshua, unto the camp, [at] Shiloh.
Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
10 And Joshua casteth for them a lot in Shiloh before Jehovah, and there Joshua apportioneth the land to the sons of Israel, according to their divisions.
Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
11 And a lot goeth up [for] the tribe of the sons of Benjamin, for their families; and the border of their lot goeth out between the sons of Judah and the sons of Joseph.
Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
12 And the border is to them at the north side from the Jordan, and the border hath gone up unto the side of Jericho on the north, and gone up through the hill-country westward, and its outgoings have been at the wilderness of Beth-Aven;
Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
13 and the border hath gone over thence to Luz, unto the side of Luz (it [is] Beth-El) southward, and the border hath gone down [to] Atroth-Addar, by the hill that [is] on the south of the lower Beth-Horon;
Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
14 and the border hath been marked out, and hath gone round to the corner of the sea southward, from the hill which [is] at the front of Beth-Horon southward, and its outgoings have been unto Kirjath-Baal (it [is] Kirjath-Jearim), a city of the sons of Judah: this [is] the west quarter.
Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
15 And the south quarter [is] from the end of Kirjath-Jearim, and the border hath gone out westward, and gone out unto the fountain of the waters of Nephtoah;
Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
16 and the border hath come down unto the extremity of the hill which [is] on the front of the valley of the son of Hinnom, which [is] in the valley of the Rephaim northward, and hath gone down the valley of Hinnom unto the side of Jebusi southward, and gone down [to] En-Rogel,
Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
17 and hath been marked out on the north, and gone out to En-Shemesh, and gone out unto Geliloth, which [is] over-against the ascent of Adummim, and gone down [to] the stone of Bohan son of Reuben,
Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
18 and passed over unto the side over-against Arabah northward, and gone down to Arabah;
Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
19 and the border hath passed over unto the side of Beth-Hoglah northward, and the outgoings of the border have been unto the north bay of the salt sea, unto the south extremity of the Jordan; this [is] the south border;
Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
20 and the Jordan doth border it at the east quarter; this [is] the inheritance of the sons of Benjamin, by its borders round about, for their families.
Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
21 And the cities for the tribe of the sons of Benjamin, for their families, have been Jericho, and Beth-Hoglah, and the valley of Keziz,
Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
22 and Beth-Arabah, Zemaraim, and Beth-El,
Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
23 and Avim, and Parah, and Ophrah,
Avimu, Para, Ofiri,
24 and Chephar-Haammonai, and Ophni, and Gaba; twelve cities and their villages.
Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
25 Gibeon, and Ramah, and Beeroth,
Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
26 and Mizpeh, and Chephirah, and Mozah,
Mizipa, Kefira, Moza
27 and Rekem, and Irpeel, and Taralah,
Rekemu, Iripeeli, Tarala,
28 and Zelah, Eleph, and Jebusi (it [is] Jerusalem), Gibeath, Kirjath: fourteen cities and their villages. This [is] the inheritance of the sons of Benjamin, for their families.
Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.

< Joshua 18 >