< Joshua 14 >

1 And these [are] they [of] the sons of Israel who inherited in the land of Canaan, whom Eleazar the priest, and Joshua son of Nun, and the heads of the fathers of the tribes of the sons of Israel, caused to inherit;
Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
2 by lot [is] their inheritance, as Jehovah commanded by the hand of Moses, for the nine of the tribes, and the half of the tribe;
Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
3 for Moses hath given the inheritance of two of the tribes, and of half of the tribe, beyond the Jordan, and to the Levites he hath not given an inheritance in their midst;
Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
4 for the sons of Joseph hath been two tribes, Manasseh and Ephraim, and they have not given a portion to the Levites in the land, except cities to dwell in, and their suburbs for their cattle, and for their possessions;
Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
5 as Jehovah commanded Moses, so have the sons of Israel done, and they apportion the land.
Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 And the sons of Judah come nigh unto Joshua in Gilgal, and Caleb son of Jephunneh the Kenezzite saith unto him, 'Thou hast known the word that Jehovah hath spoken unto Moses the man of God, concerning me and concerning thee in Kadesh-Barnea:
Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
7 a son of forty years [am] I in Moses, servant of Jehovah, sending me from Kadesh-Barnea, to spy the land, and I bring him back word as with my heart;
Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
8 and my brethren who have gone up with me have caused the heart of the people to melt, and I have been fully after Jehovah my God;
Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
9 and Moses sweareth in that day, saying, If not — the land on which thy foot hath trodden, to thee it is for inheritance, and to thy sons — to the age, for thou hast been fully after Jehovah my God.
Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
10 'And, now, lo, Jehovah hath kept me alive, as He hath spoken, these forty and five years, since Jehovah spake this word unto Moses, when Israel went in the wilderness; and now, lo, I [am] to-day a son of five and eighty years;
“Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
11 yet [am] I to-day strong as in the day of Moses' sending me; as my power then, so [is] my power now, for battle, and to go out, and to come in.
Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
12 'And now, give to me this hill-country, of which Jehovah spake in that day, for thou didst hear in that day, for Anakim [are] there, and cities, great, fenced; if so be Jehovah [is] with me, then I have dispossessed them, as Jehovah hath spoken.'
Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
13 And Joshua blesseth him, and giveth Hebron to Caleb son of Jephunneh for an inheritance,
Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
14 therefore hath Hebron been to Caleb son of Jephunneh the Kenezzite for an inheritance unto this day, because that he was fully after Jehovah, God of Israel;
Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
15 and the name of Hebron formerly [is] Kirjath-Arba (he [is] the great man among the Anakim); and the land hath rest from war.
(Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.

< Joshua 14 >