< Job 37 >

1 Also, at this my heart trembleth, And it moveth from its place.
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Hearken diligently to the trembling of His voice, Yea, the sound from His mouth goeth forth.
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 Under the whole heavens He directeth it, And its light [is] over the skirts of the earth.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 After it roar doth a voice — He thundereth with the voice of His excellency, And He doth not hold them back, When His voice is heard.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 God thundereth with His voice wonderfully, Doing great things and we know not.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 For to snow He saith, 'Be [on] the earth.' And the small rain and great rain of His power.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 Into the hand of every man he sealeth, For the knowledge by all men of His work.
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 And enter doth the beast into covert, And in its habitations it doth continue.
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 From the inner chamber cometh a hurricane, And from scatterings winds — cold,
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 From the breath of God is frost given, And the breadth of waters is straitened,
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Yea, by filling He doth press out a cloud, Scatter a cloud doth His light.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 And it is turning itself round by His counsels, For their doing all He commandeth them, On the face of the habitable earth.
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Whether for a rod, or for His land, Or for kindness — He doth cause it to come.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 Hear this, O Job, Stand and consider the wonders of God.
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Dost thou know when God doth place them, And caused to shine the light of His cloud?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Dost thou know the balancings of a cloud? The wonders of the Perfect in knowledge?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 How thy garments [are] warm, In the quieting of the earth from the south?
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 Thou hast made an expanse with Him For the clouds — strong as a hard mirror!
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 Let us know what we say to Him, We set not in array because of darkness.
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Is it declared to Him that I speak? If a man hath spoken, surely he is swallowed up.
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 And now, they have not seen the light, Bright it [is] in the clouds, And the wind hath passed by and cleanseth them.
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 From the golden north it cometh, Beside God [is] fearful honour.
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 The Mighty! we have not found Him out, High in power and judgment, He doth not answer! And abundant in righteousness,
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Therefore do men fear Him, He seeth not any of the wise of heart.
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

< Job 37 >