< Job 34 >

1 And Elihu answereth and saith:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Hear, O wise men, my words, And, O knowing ones, give ear to me.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 For the ear doth try words, And the palate tasteth to eat.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Judgment let us choose for ourselves, Let us know among ourselves what [is] good.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 For Job hath said, 'I have been righteous, And God hath turned aside my right,
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Against my right do I lie? Mortal [is] mine arrow — without transgression.'
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Who [is] a man like Job? He drinketh scoffing like water,
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 And he hath travelled for company With workers of iniquity, So as to go with men of wickedness.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 For he hath said, 'It doth not profit a man, When he delighteth himself with God.'
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Therefore, O men of heart, hearken to me; Far be it from God to do wickedness, And [from] the Mighty to do perverseness:
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 For the work of man he repayeth to him, And according to the path of each He doth cause him to find.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Yea, truly, God doth not do wickedly, And the Mighty doth not pervert judgment.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Who hath inspected for Himself the earth? And who hath placed all the habitable world?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 If He doth set on him His heart, His spirit and his breath unto Him He gathereth.
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 Expire doth all flesh together, And man to dust returneth.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 And if [there is] understanding, hear this, Give ear to the voice of my words.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Yea, doth one hating justice govern? Or the Most Just dost thou condemn?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Who hath said to a king — 'Worthless,' Unto princes — 'Wicked?'
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 That hath not accepted the person of princes, Nor hath known the rich before the poor, For a work of His hands [are] all of them.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 [In] a moment they die, and at midnight Shake do people, and they pass away, And they remove the mighty without hand.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 For His eyes [are] on the ways of each, And all his steps He doth see.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 There is no darkness nor death-shade, For workers of iniquity to be hidden there;
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 For He doth not suffer man any more, To go unto God in judgment,
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 He breaketh the mighty — no searching! And He appointeth others in their stead.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Therefore He knoweth their works, And He hath overturned by night, And they are bruised.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 As wicked He hath stricken them, In the place of beholders.
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Because that against right They have turned aside from after Him, And none of His ways have considered wisely,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 To cause to come in unto Him The cry of the poor, And the cry of the afflicted He heareth.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 And He giveth rest, and who maketh wrong? And hideth the face, and who beholdeth it? And in reference to a nation and to a man, [It is] the same.
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 From the reigning of a profane man, From the snares of a people;
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 For unto God hath any said: 'I have taken away, I do not corruptly,
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Besides [that which] I see, shew Thou me, If iniquity I have done — I do not add?'
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 By thee doth He recompense, That thou hast refused — That thou dost choose, and not I? And what thou hast known, speak.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Let men of heart say to me, And a wise man is hearkening to me.
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 Job — not with knowledge doth he speak, And his words [are] not with wisdom.
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 My Father! let Job be tried — unto victory, Because of answers for men of iniquity,
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 For he doth add to his sin, Transgression among us he vomiteth, And multiplieth his sayings to God.
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >