< Job 21 >
1 And Job answereth and saith: —
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hear ye diligently my word, And this is your consolation.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Bear with me, and I speak, And after my speaking — ye may deride.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 I — to man [is] my complaint? and if [so], wherefore May not my temper become short?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Turn unto me, and be astonished, And put hand to mouth.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Yea, if I have remembered, then I have been troubled. And my flesh hath taken fright.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Wherefore do the wicked live? They have become old, Yea, they have been mighty in wealth.
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Their seed is established, Before their face with them, And their offspring before their eyes.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Their houses [are] peace without fear, Nor [is] a rod of God upon them.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 His bullock hath eaten corn, and doth not loath. His cow bringeth forth safely, And doth not miscarry.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 They send forth as a flock their sucklings, And their children skip,
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 They lift [themselves] up at timbrel and harp, And rejoice at the sound of an organ.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 They wear out in good their days, And in a moment [to] Sheol go down. (Sheol )
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol )
14 And they say to God, 'Turn aside from us, And the knowledge of Thy ways We have not desired.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 What [is] the Mighty One that we serve Him? And what do we profit when we meet with Him?'
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Lo, not in their hand [is] their good, (The counsel of the wicked Hath been far from me.)
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 How oft is the lamp of the wicked extinguished, And come on them doth their calamity? Pangs He apportioneth in His anger.
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 They are as straw before wind, And as chaff a hurricane hath stolen away,
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 God layeth up for his sons his sorrow, He giveth recompense unto him — and he knoweth.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 His own eyes see his destruction, And of the wrath of the Mighty he drinketh.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For what [is] his delight in his house after him, And the number of his months cut off?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 To God doth [one] teach knowledge, And He the high doth judge?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 This [one] dieth in his perfect strength, Wholly at ease and quiet.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 His breasts have been full of milk, And marrow his bones doth moisten.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 And this [one] dieth with a bitter soul, And have not eaten with gladness.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Together — on the dust they lie down, And the worm doth cover them over.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Lo, I have known your thoughts, And the devices against me ye do wrongfully.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 For ye say, 'Where [is] the house of the noble? And where the tent — The tabernacles of the wicked?'
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Have ye not asked those passing by the way? And their signs do ye not know?
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 That to a day of calamity is the wicked spared. To a day of wrath they are brought.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who doth declare to his face his way? And [for] that which he hath done, Who doth give recompence to him?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 And he — to the graves he is brought. And over the heap a watch is kept.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Sweet to him have been the clods of the valley, And after him every man he draweth, And before him there is no numbering.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 And how do ye comfort me [with] vanity, And in your answers hath been left trespass?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”