< Job 18 >

1 And Bildad the Shuhite answereth and saith: —
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 When do ye set an end to words? Consider ye, and afterwards do we speak.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Wherefore have we been reckoned as cattle? We have been defiled in your eyes!
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 (He is tearing himself in his anger.) For thy sake is earth forsaken? And removed is a rock from its place?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Also, the light of the wicked is extinguished. And there doth not shine a spark of his fire.
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 The light hath been dark in his tent, And his lamp over him is extinguished.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 Straitened are the steps of his strength, And cast him down doth his own counsel.
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 For he is sent into a net by his own feet, And on a snare he doth walk habitually.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 Seize on the heel doth a gin, Prevail over him do the designing.
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Hidden in the earth is his cord, And his trap on the path.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Round about terrified him have terrors, And they have scattered him — at his feet.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Hungry is his sorrow, And calamity is ready at his side.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 It consumeth the parts of his skin, Consume his parts doth death's first-born.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Drawn from his tent is his confidence, And it causeth him to step to the king of terrors.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 It dwelleth in his tent — out of his provender, Scattered over his habitation is sulphur.
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 From beneath his roots are dried up, And from above cut off is his crop.
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 His memorial hath perished from the land, And he hath no name on the street.
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 They thrust him from light unto darkness, And from the habitable earth cast him out.
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 He hath no continuator, Nor successor among his people, And none is remaining in his dwellings.
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 At this day westerns have been astonished And easterns have taken fright.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Only these [are] tabernacles of the perverse, And this the place God hath not known.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >