< Job 17 >

1 My spirit hath been destroyed, My days extinguished — graves [are] for me.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 If not — mockeries [are] with me. And in their provocations mine eye lodgeth.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Place, I pray Thee, my pledge with Thee; Who is he that striketh hand with me?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 For their heart Thou hast hidden From understanding, Therefore Thou dost not exalt them.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 For a portion he sheweth friendship, And the eyes of his sons are consumed.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 And he set me up for a proverb of the peoples, And a wonder before them I am.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 And dim from sorrow is mine eye, And my members as a shadow all of them.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Astonished are the upright at this, And the innocent against the profane Stirreth himself up.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 And the righteous layeth hold [on] his way, And the clean of hands addeth strength, And — dumb are they all.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Return, and come in, I pray you, And I find not among you a wise man.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 My days have passed by, My devices have been broken off, The possessions of my heart!
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Night for day they appoint, Light [is] near because of darkness.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 If I wait — Sheol [is] my house, In darkness I have spread out my couch. (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 To corruption I have called: — 'Thou [art] my father.' 'My mother' and 'my sister' — to the worm.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 And where [is] now my hope? Yea, my hope, who doth behold it?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 [To] the parts of Sheol ye go down, If together on the dust we may rest. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Job 17 >