< Job 12 >

1 And Job answereth and saith: —
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Truly — ye [are] the people, And with you doth wisdom die.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 I also have a heart like you, I am not fallen more than you, And with whom is there not like these?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 A laughter to his friend I am: 'He calleth to God, and He answereth him,' A laughter [is] the perfect righteous one.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 A torch — despised in the thoughts of the secure Is prepared for those sliding with the feet.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 At peace are the tents of spoilers, And those provoking God have confidence, He into whose hand God hath brought.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 And yet, ask, I pray thee, [One of] the beasts, and it doth shew thee, And a fowl of the heavens, And it doth declare to thee.
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Or talk to the earth, and it sheweth thee, And fishes of the sea recount to thee:
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 'Who hath not known in all these, That the hand of Jehovah hath done this?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 In whose hand [is] the breath of every living thing, And the spirit of all flesh of man.'
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Doth not the ear try words? And the palate taste food for itself?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 With the very aged [is] wisdom, And [with] length of days understanding.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 With Him [are] wisdom and might, To him [are] counsel and understanding.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Lo, He breaketh down, and it is not built up, He shutteth against a man, And it is not opened.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Lo, He keepeth in the waters, and they are dried up, And he sendeth them forth, And they overturn the land.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 With Him [are] strength and wisdom, His the deceived and deceiver.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Causing counsellors to go away a spoil, And judges He maketh foolish.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 The bands of kings He hath opened, And He bindeth a girdle on their loins.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Causing ministers to go away a spoil And strong ones He overthroweth.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Turning aside the lip of the stedfast, And the reason of the aged He taketh away.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Pouring contempt upon princes, And the girdle of the mighty He made feeble.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Removing deep things out of darkness, And He bringeth out to light death-shade.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Magnifying the nations, and He destroyeth them, Spreading out the nations, and He quieteth them.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Turning aside the heart Of the heads of the people of the land, And he causeth them to wander In vacancy — no way!
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 They feel darkness, and not light, He causeth them to wander as a drunkard.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Job 12 >