< Genesis 8 >
1 And God remembereth Noah, and every living thing, and all the cattle which [are] with him in the ark, and God causeth a wind to pass over the earth, and the waters subside,
Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
2 and closed are the fountains of the deep and the net-work of the heavens, and restrained is the shower from the heavens.
Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
3 And turn back do the waters from off the earth, going on and returning; and the waters are lacking at the end of a hundred and fifty days.
Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
4 And the ark resteth, in the seventh month, in the seventeenth day of the month, on mountains of Ararat;
ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
5 and the waters have been going and becoming lacking till the tenth month; in the tenth [month], on the first of the month, appeared the heads of the mountains.
Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
6 And it cometh to pass, at the end of forty days, that Noah openeth the window of the ark which he made,
Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
7 and he sendeth forth the raven, and it goeth out, going out and turning back till the drying of the waters from off the earth.
natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
8 And he sendeth forth the dove from him to see whether the waters have been lightened from off the face of the ground,
Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
9 and the dove hath not found rest for the sole of her foot, and she turneth back unto him, unto the ark, for waters [are] on the face of all the earth, and he putteth out his hand, and taketh her, and bringeth her in unto him, unto the ark.
Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
10 And he stayeth yet other seven days, and addeth to send forth the dove from the ark;
Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
11 and the dove cometh in unto him at even-time, and lo, an olive leaf torn off in her mouth; and Noah knoweth that the waters have been lightened from off the earth.
Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
12 And he stayeth yet other seven days, and sendeth forth the dove, and it added not to turn back unto him any more.
Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
13 And it cometh to pass in the six hundredth and first year, in the first [month], in the first of the month, the waters have been dried from off the earth; and Noah turneth aside the covering of the ark, and looketh, and lo, the face of the ground hath been dried.
Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
14 And in the second month, in the seven and twentieth day of the month, the earth hath become dry.
Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
15 And God speaketh unto Noah, saying, 'Go out from the ark, thou, and thy wife, and thy sons, and thy sons' wives with thee;
Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
16 every living thing that [is] with thee, of all flesh, among fowl, and among cattle, and among every creeping thing which is creeping on the earth, bring out with thee;
“Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
17 and they have teemed in the earth, and been fruitful, and have multiplied on the earth.'
Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
18 And Noah goeth out, and his sons, and his wife, and his sons' wives with him;
Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
19 every beast, every creeping thing, and every fowl; every creeping thing on the earth, after their families, have gone out from the ark.
Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
20 And Noah buildeth an altar to Jehovah, and taketh of every clean beast, and of every clean fowl, and causeth burnt-offerings to ascend on the altar;
Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
21 and Jehovah smelleth the sweet fragrance, and Jehovah saith unto His heart, 'I continue not to disesteem any more the ground because of man, though the imagination of the heart of man [is] evil from his youth; and I continue not to smite any more all living, as I have done;
Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
22 during all days of the earth, seed-time and harvest, and cold and heat, and summer and winter, and day and night, do not cease.'
“Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”