< Genesis 50 >
1 And Joseph falleth on his father's face, and weepeth over him, and kisseth him;
Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
2 and Joseph commandeth his servants, the physicians, to embalm his father, and the physicians embalm Israel;
Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
3 and they fulfil for him forty days, for so they fulfil the days of the embalmed, and the Egyptians weep for him seventy days.
Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
4 And the days of his weeping pass away, and Joseph speaketh unto the house of Pharaoh, saying, 'If, I pray you, I have found grace in your eyes, speak, I pray you, in the ears of Pharaoh, saying,
Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
5 My father caused me to swear, saying, Lo, I am dying; in my burying-place which I have prepared for myself in the land of Canaan, there dost thou bury me; and now, let me go up, I pray thee, and bury my father, and return;'
‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
6 and Pharaoh saith, 'Go up and bury thy father, as he caused thee to swear.'
Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
7 And Joseph goeth up to bury his father, and go up with him do all the servants of Pharaoh, elders of his house, and all the elders of the land of Egypt,
Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
8 and all the house of Joseph, and his brethren, and the house of his father; only their infants, and their flock, and their herd, have they left in the land of Goshen;
Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
9 and there go up with him both chariot and horsemen, and the camp is very great.
Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
10 And they come unto the threshing-floor of Atad, which [is] beyond the Jordan, and they lament there, a lamentation great and very grievous; and he maketh for his father a mourning seven days,
Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
11 and the inhabitant of the land, the Canaanite, see the mourning in the threshing-floor of Atad, and say, 'A grievous mourning [is] this to the Egyptians;' therefore hath [one] called its name 'The mourning of the Egyptians,' which [is] beyond the Jordan.
Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
12 And his sons do to him so as he commanded them,
Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
13 and his sons bear him away to the land of Canaan, and bury him in the cave of the field of Machpelah, which Abraham bought with the field for a possession of a burying-place, from Ephron the Hittite, on the front of Mamre.
Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
14 And Joseph turneth back to Egypt, he and his brethren, and all who are going up with him to bury his father, after his burying his father.
Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
15 And the brethren of Joseph see that their father is dead, and say, 'Peradventure Joseph doth hate us, and doth certainly return to us all the evil which we did with him.'
Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
16 And they give a charge for Joseph, saying, 'Thy father commanded before his death, saying,
Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
17 Thus ye do say to Joseph, I pray thee, bear, I pray thee, with the transgression of thy brethren, and their sin, for they have done thee evil; and now, bear, we pray thee, with the transgression of the servants of the God of thy father;' and Joseph weepeth in their speaking unto him.
‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
18 And his brethren also go and fall before him, and say, 'Lo, we [are] to thee for servants.'
Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
19 And Joseph saith unto them, 'Fear not, for [am] I in the place of God?
Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
20 As for you, ye devised against me evil — God devised it for good, in order to do as [at] this day, to keep alive a numerous people;
Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
21 and now, fear not: I do nourish you and your infants;' and he comforteth them, and speaketh unto their heart.
Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
22 And Joseph dwelleth in Egypt, he and the house of his father, and Joseph liveth a hundred and ten years,
Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
23 and Joseph looketh on Ephraim's sons of the third [generation]; sons also of Machir, son of Manasseh, have been born on the knees of Joseph.
ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
24 And Joseph saith unto his brethren, 'I am dying, and God doth certainly inspect you, and hath caused you to go up from this land, unto the land which He hath sworn to Abraham, to Isaac, and to Jacob.'
Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
25 And Joseph causeth the sons of Israel to swear, saying, 'God doth certainly inspect you, and ye have brought up my bones from this [place].'
Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
26 And Joseph dieth, a son of an hundred and ten years, and they embalm him, and he is put into a coffin in Egypt.
Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.