< Genesis 21 >
1 And Jehovah hath looked after Sarah as He hath said, and Jehovah doth to Sarah as He hath spoken;
Yehova anakomera mtima Sara monga ananenera, ndipo Yehovayo anachita monga momwe analonjezera.
2 and Sarah conceiveth, and beareth a son to Abraham, to his old age, at the appointed time that God hath spoken of with him;
Sara anakhala ndi pathupi ndipo anamuberekera Abrahamu mwana wamwamuna mu ukalamba wake, pa nyengo imene Mulungu anamulonjeza.
3 and Abraham calleth the name of his son who is born to him, whom Sarah hath born to him — Isaac;
Abrahamu anapereka dzina loti Isake kwa mwana wamwamuna amene Sara anamuberekera.
4 and Abraham circumciseth Isaac his son, [being] a son of eight days, as God hath commanded him.
Isake atakwanitsa masiku asanu ndi atatu, Abrahamu anamuchita mdulidwe monga Mulungu anamulamulira.
5 And Abraham [is] a son of a hundred years in Isaac his son being born to him,
Abrahamu anali ndi 100 pamene mwana wake Isake anabadwa.
6 and Sarah saith, 'God hath made laughter for me; every one who is hearing laugheth for me.'
Sara anati, “Mulungu wandibweretsera mseko, ndipo aliyense amene adzamva zimenezi adzaseka nane pamodzi.”
7 She saith also, 'Who hath said to Abraham, Sarah hath suckled sons, that I have born a son for his old age?'
Ndipo anawonjezera kuti, “Ndani akanamuwuza Abrahamu kuti Sara nʼkudzayamwitsako ana? Chonsecho ndamubalira mwana wamwamuna kuwukalamba wake.”
8 And the lad groweth, and is weaned, and Abraham maketh a great banquet in the day of Isaac's being weaned;
Mwana uja anakula mpaka kumuletsa kuyamwa. Tsiku lomuletsa Isake kuyamwa, Abrahamu anakonza phwando lalikulu.
9 and Sarah seeth the son of Hagar the Egyptian, whom she hath borne to Abraham, mocking,
Koma Sara anaona kuti mwana wamwamuna amene Hagara Mwigupto anamuberekera Abrahamu amamuseka,
10 and she saith to Abraham, 'Cast out this handmaid and her son; for the son of this handmaid hath no possession with my son — with Isaac.'
ndipo anati kwa Abrahamu, “Muchotse mdzakazi ndi mwana wake wamwamunayu, pakuti mwana wa kapolo sadzagawana chuma ndi mwana wanga Isake.”
11 And the thing is very wrong in the eyes of Abraham, for his son's sake;
Nkhaniyi inamumvetsa chisoni kwambiri Abrahamu chifukwa imakhudza mwana wake.
12 and God saith unto Abraham, 'Let it not be wrong in thine eyes because of the youth, and because of thy handmaid: all that Sarah saith unto thee — hearken to her voice, for in Isaac is a seed called to thee.
Koma Mulungu anamuwuza Abrahamu kuti, “Usamve chisoni motero ndi mnyamatayu ndi mdzakazi wakoyu. Mvetsera chilichonse chomwe Sara akukuwuza, chifukwa zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
13 As to the son of the handmaid also, for a nation I set him, because he [is] thy seed.'
Mwana wa mdzakazi wakoyu ndidzamusandutsa mtundu wa anthu chifukwa ndi mwana wako.”
14 And Abraham riseth early in the morning, and taketh bread, and a bottle of water, and giveth unto Hagar (placing [it] on her shoulder), also the lad, and sendeth her out; and she goeth on, and goeth astray in the wilderness of Beer-Sheba;
Mmamawa wake, Abrahamu anatenga chakudya ndi botolo la madzi nazipereka kwa Hagara. Anasenzetsa Hagara nawaperekeza pangʼono ndi mnyamatayo. Hagara ananyamuka nayendayenda mʼchipululu cha Beeriseba.
15 and the water is consumed from the bottle, and she placeth the lad under one of the shrubs.
Madzi atatha mʼbotolo muja, anamuyika mnyamatayo pansi pa zitsamba.
16 And she goeth and sitteth by herself over-against, afar off, about a bow-shot, for she said, 'Let me not look on the death of the lad;' and she sitteth over-against, and lifteth up her voice, and weepeth.
Kenaka Hagara anachoka nakakhala pansi cha pakatalipo, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi, popeza mʼmaganizo mwake amati, “Sindingaonerere mwanayu akufa.” Ndipo anakhala pansi cha poteropo nʼkumalira.
17 And God heareth the voice of the youth; and the messenger of God calleth unto Hagar from the heavens, and saith to her, 'What to thee, Hagar? fear not; for God hath hearkened unto the voice of the youth where he [is];
Mulungu anamva mnyamatayo akulira ndipo mngelo wa Mulungu anayankhula kwa Hagara kuchokera kumwamba nati, “Chavuta nʼchiyani Hagara? Usachite mantha; Mulungu wamva kulira kwa mnyamatayo pamene wagonapo.
18 rise, lift up the youth, and lay hold on him with thy hand, for for a great nation I set him.'
Munyamule mnyamatayo ndipo umugwire dzanja pakuti ndidzamupanga kukhala mtundu waukulu.”
19 And God openeth her eyes, and she seeth a well of water, and she goeth and filleth the bottle [with] water, and causeth the youth to drink;
Kenaka Mulungu anatsekula maso a Hagara ndipo anaona chitsime cha madzi. Choncho anapita nadzaza botolo lija ndi madzi ndi kumupatsa mnyamatayo kuti amwe.
20 and God is with the youth, and he groweth, and dwelleth in the wilderness, and is an archer;
Mulungu anali ndi mnyamatayo pamene ankakula. Anakhala ku chipululu nakhala katswiri wolasa uta.
21 and he dwelleth in the wilderness of Paran, and his mother taketh for him a wife from the land of Egypt.
Akukhala ku chipululu cha Parani, mayi ake anamupezera mkazi wochokera ku Igupto.
22 And it cometh to pass at that time that Abimelech speaketh — Phichol also, head of his host — unto Abraham, saying, 'God [is] with thee in all that thou art doing;
Pa nthawiyo, Abimeleki ndi Fikolo wamkulu wankhondo wake anati kwa Abrahamu, “Mulungu ali nawe pa chilichonse umachita.
23 and now, swear to me by God here: thou dost not lie to me, or to my continuator, or to my successor; according to the kindness which I have done with thee thou dost with me, and with the land in which thou hast sojourned.'
Tsopano undilumbirire ine pano pamaso pa Mulungu kuti sudzachita mwa chinyengo ndi ine kapena ana anga kapena zidzukulu zanga. Undionetse ine pamodzi ndi dziko limene ukukhalamo ngati mlendo, kukoma mtima kokhala ngati kumene ndinakuonetsa ine.”
24 And Abraham saith, 'I — I do swear.'
Abrahamu anati, “Ine ndikulumbira.”
25 And Abraham reasoned with Abimelech concerning the matter of a well of water which Abimelech's servants have taken violently away,
Kenaka Abrahamu anadandaula kwa Abimeleki pa za chitsime chimene antchito a Abimeleki analanda.
26 and Abimelech saith, 'I have not known who hath done this thing, and even thou didst not declare to me, and I also, I have not heard save to-day.'
Koma Abimeleki anati, “Ine sindikudziwa amene anachita zimenezi. Iwe sunandiwuze, ndipo ndazimva lero zimenezi.”
27 And Abraham taketh sheep and oxen, and giveth to Abimelech, and they make, both of them, a covenant;
Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.
28 and Abraham setteth seven Lambs of the flock by themselves.
Abrahamu anapatulako ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri kuchoka pagulu la nkhosa zina,
29 And Abimelech saith unto Abraham, 'What [are] they — these seven lambs which thou hast set by themselves?'
ndipo Abimeleki anafunsa Abrahamu, “Kodi tanthauzo lake la ana ankhosa aakazi asanu ndi awiri amene wawapatula pawokhawa nʼchiyani?”
30 And he saith, 'For — the seven lambs thou dost accept from my hand, so that it becometh a witness for me that I have digged this well;'
Iye anayankha kuti, “Landirani ana ankhosa aakazi kuchokera mʼdzanja langa ngati umboni kuti ndinakumba chitsime ichi.”
31 therefore hath he called that place 'Beer-Sheba,' for there have both of them sworn.
Kotero malo amenewo anatchedwa Beeriseba, chifukwa anthu awiriwo analumbirirapo malumbiro.
32 And they make a covenant in Beer-Sheba, and Abimelech riseth — Phichol also, head of his host — and they turn back unto the land of the Philistines;
Atatha kuchita pangano pa Beeriseba, Abimeleki ndi Fikolo mkulu wankhondo wake anabwerera ku dziko la Afilisti.
33 and [Abraham] planteth a tamarisk in Beer-Sheba, and preacheth there in the name of Jehovah, God age-during;
Abrahamu anadzala mtengo wa bwemba ku Beeriseba, ndipo anapemphera pamenepo mʼdzina la Yehova, Mulungu Wamuyaya.
34 and Abraham sojourneth in the land of the Philistines many days.
Ndipo Abrahamu anakhala mʼdziko la Afilisti kwa nthawi yayitali.