< Ezekiel 10 >
1 And I look, and lo, on the expanse that [is] above the head of the cherubs, as a sapphire stone, as the appearance of the likeness of a throne, He hath been seen over them.
Ine nditayangʼana ku thambo limene lili pamwamba pa mitu ya akerubi ndinangoona chinthu chooneka ngati mpando waufumu wa mwala wa safiro.
2 And He speaketh unto the man clothed with linen, and saith, 'Go in unto the midst of the wheel, unto the place of the cherub, and fill thy hands with coals of fire from between the cherubs, and scatter over the city.' And he goeth in before mine eyes.
Tsono Yehova anawuza munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pita pakati pa mikombero kunsi kwa akerubi. Udzaze manja ako ndi makala oyaka amene ali pakati pa akerubiwo ndipo uwawaze mu mzinda.” Iye anachita zimenezi ine ndikuona.
3 And the cherubs are standing on the right side of the house, at the going in of the man, and the cloud hath filled the inner court,
Apa akerubiwo anali atayima mbali ya kummwera kwa Nyumba ya Mulungu pamene munthuyo ankalowa. Tsono mtambo unadzaza bwalo lamʼkati.
4 and become high doth the honour of Jehovah above the cherub, over the threshold of the house, and the house is filled with the cloud, and the court hath been filled with the brightness of the honour of Jehovah.
Ndipo ulemerero wa Yehova unachoka pamwamba pa akerubi ndipo unafika ku chiwundo cha Nyumba ya Mulungu. Mtambo unadzaza Nyumba ya Mulungu, ndipo kuwala kwa ulemerero wa Yehova kunadzaza bwalolo.
5 And a noise of the wings of the cherubs hath been heard unto the outer court, as the voice of God — the Mighty One — in His speaking.
Phokoso la mapiko a akerubi limamveka mpaka ku bwalo lakunja, monga momwe linamvekera liwu la Mulungu Wamphamvuzonse akamayankhula.
6 And it cometh to pass, in His commanding the man clothed with linen, saying, 'Take fire from between the wheel, from between the cherubs,' and he goeth in and standeth near the wheel,
Kenaka Yehova analamula munthu wovala chovala chabafuta uja kuti, “Pala moto pakati pa mikombero, pakati pa akerubi.” Munthu uja anapitadi nakayima pa mbali pa mkombero umodzi.
7 that the [one] cherub putteth forth his hand from between the cherubs unto the fire that [is] between the cherubs, and lifteth up, and giveth into the hands of him who is clothed with linen, and he receiveth, and cometh forth.
Ndipo mmodzi wa akerubi anatambalitsa dzanja lake mpaka pa moto umene unali pakati pawo. Iye anapalako motowo ndipo anapatsa munthu wovala chovala chabafuta uja. Tsono iye anawulandira natuluka.
8 And there appeareth in the cherubs the form of a hand of man under their wings,
Ndiye kuti kunsi kwa mapiko akerubi kumaoneka zinthu zooneka ngati manja a munthu.
9 and I look, and lo, four wheels near the cherubs, one wheel near the one cherub, and another wheel near the other cherub, and the appearance of the wheels [is] as the colour of a beryl stone.
Ine nditayangʼanitsitsa ndinaona mikombero inayi pambali pa akerubi. Pambali pa kerubi aliyense panali mkombero umodzi; mikomberoyo inkanyezimira ngati miyala yokongola ya krizoliti.
10 As to their appearances, one likeness [is] to them four, as it were the wheel in the midst of the wheel.
Maonekedwe a mikombero inayi ija anali ofanana. Mkombero uliwonse umaoneka ngati mkombero wolowana ndi unzake.
11 In their going, on their four sides they go; they turn not round in their going, for to the place whither the head turneth, after it they go, they turn not round in their going.
Poyenda akerubiwo, amapita mbali iliyonse ya mbali zinayizo kumene akerubiwo amayangʼana. Mikomberoyo simatembenuka pamene akerubiwo ankayenda. Kulikonse kumene mutu walunjika nʼkumene ankapita popanda kutembenuka.
12 And all their flesh, and their backs, and their hands, and their wings, and the wheels, are full of eyes round about; to them four [are] their wheels.
Matupi awo onse, misana yawo, manja awo ndi mapiko awo zinali ndi maso okhaokha, monganso mʼmene inalili mikombero yawo inayi ija.
13 To the wheels — to them is one calling in mine ears, 'O wheel!'
Ine ndinamva mikombero ikutchedwa kuti, “mikombero yakamvuluvulu.”
14 And four faces [are] to each; the face of the one [is] the face of the cherub, and the face of the second the face of man, and of the third the face of a lion, and of the fourth the face of an eagle.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi. Nkhope yoyamba inali ya Kerubi, nkhope yachiwiri inali ya munthu, nkhope yachitatu inali ya mkango ndipo nkhope yachinayi inali ya chiwombankhanga.
15 And the cherubs are lifted up, it [is] the living creature that I saw by the river Chebar.
Tsono akerubi aja anawuluka. Izi zinali zamoyo zija zimene ndinaziona ku mtsinje wa Kebara.
16 And in the going of the cherubs, the wheels go beside them; and in the cherubs lifting up their wings to be high above the earth, the wheels turn not round, even they, from being beside them.
Pamene akerubi ankayenda, nayonso mikombero ya mʼmbali mwawo inkayenda. Akerubiwo ankati akatambasula mapiko awo kuti auluke mikombero sinkachoka mʼmbali mwawo.
17 In their standing they stand, and in their exaltation they are exalted with them: for the living spirit [is] in them.
Akerubiwo ankati akayima, mikombero inkayimanso. Ngati akerubiwo auluka, mikomberoyo inkapita nawo chifukwa mzimu wa zamoyozo ndiwo unkayendetsa mikomberoyo.
18 And go forth doth the honour of Jehovah from off the threshold of the house, and standeth over the cherubs,
Pamenepo ulemerero wa Yehova unachoka pa chiwundo cha Nyumba ya Mulungu ndi kukakhala pamwamba pa akerubi.
19 and the cherubs lift up their wings, and are lifted up from the earth before mine eyes; in their going forth, the wheels also [are] over-against them, and he standeth at the opening of the east gate of the house of Jehovah, and the honour of the God of Israel [is] over them from above.
Ine ndikuona akerubi, anatambasula mapiko awo ndi kuwuluka. Pamene ankapita, mikombero inapita nawo pamodzi. Akerubi anakayima pa khomo la chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Tsono ulemerero wowala wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
20 It [is] the living creature that I saw under the God of Israel by the river Chebar, and I know that they are cherubs.
Izi ndizo zamoyo ndinaziona pansi pa Mulungu wa Israeli ku mtsinje wa Kebara, ndipo ndinazindikira kuti anali akerubi.
21 Four faces [are] to each, and four wings to each, and the likeness of the hands of man [is] under their wings.
Kerubi aliyense anali ndi nkhope zinayi ndi mapiko anayi, ndipo kunsi kwa mapiko awo kunali chinthu chimene chimaoneka ngati manja a munthu.
22 As to the likeness of their faces, they [are] the faces that I saw by the river Chebar, their appearances and themselves; each straight forward they go.
Nkhope zawo zinali zofanana ndi zomwe ndinaziona ku mtsinje wa Kebara. Kerubi aliyense amayenda molunjika.