< Deuteronomy 15 >
1 'At the end of seven years thou dost make a release,
Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
2 and this [is] the matter of the release: Every owner of a loan [is] to release his hand which he doth lift up against his neighbour, he doth not exact of his neighbour and of his brother, but hath proclaimed a release to Jehovah;
Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
3 of the stranger thou mayest exact, and that which is thine with thy brother doth thy hand release;
Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
4 only when there is no needy one with thee, for Jehovah doth greatly bless thee in the land which Jehovah thy God is giving to thee — an inheritance to possess it.
Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
5 'Only, if thou dost diligently hearken to the voice of Jehovah thy God, to observe to do all this command which I am commanding thee to-day,
Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
6 for Jehovah thy God hath blessed thee as He hath spoken to thee; and thou hast lent [to] many nations, and thou hast not borrowed; and thou hast ruled over many nations, and over thee they do not rule.
Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
7 'When there is with thee any needy one of one of thy brethren, in one of thy cities, in thy land which Jehovah thy God is giving to thee, thou dost not harden thy heart, nor shut thy hand from thy needy brother;
Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
8 for thou dost certainly open thy hand to him, and dost certainly lend him sufficient for his lack which he lacketh.
Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
9 'Take heed to thee lest there be a word in thy heart — worthless, saying, Near [is] the seventh year, the year of release; and thine eye is evil against thy needy brother, and thou dost not give to him, and he hath called concerning thee unto Jehovah, and it hath been in thee sin;
Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
10 thou dost certainly give to him, and thy heart is not sad in thy giving to him, for because of this thing doth Jehovah thy God bless thee in all thy works, and in every putting forth of thy hand;
Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
11 because the needy one doth not cease out of the land, therefore I am commanding thee, saying, Thou dost certainly open thy hand to thy brother, to thy poor, and to thy needy one, in thy land.
Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
12 'When thy brother is sold to thee, a Hebrew or a Hebrewess, and he hath served thee six years — then in the seventh year thou dost send him away free from thee.
Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
13 And when thou dost send him away free from thee, thou dost not send him away empty;
Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
14 thou dost certainly encircle him out of thy flock, and out of thy threshing-floor, and out of thy wine-vat; [of] that which Jehovah thy God hath blessed thee thou dost give to him,
Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
15 and thou hast remembered that a servant thou hast been in the land of Egypt, and Jehovah thy God doth ransom thee; therefore I am commanding thee this thing to-day.
Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
16 'And it hath been, when he saith unto thee, I go not out from thee — because he hath loved thee, and thy house, because [it is] good for him with thee —
Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
17 then thou hast taken the awl, and hast put [it] through his ear, and through the door, and he hath been to thee a servant age-during; and also to thy handmaid thou dost do so.
pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
18 'It is not hard in thine eyes, in thy sending him away free from thee; for the double of the hire of an hireling he hath served thee six years, and Jehovah thy God hath blessed thee in all that thou dost.
Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
19 'Every firstling that is born in thy herd and in thy flock — the male thou dost sanctify to Jehovah thy God; thou dost not work with the firstling of thine ox, nor shear the firstling of thy flock;
Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
20 before Jehovah thy God thou dost eat it year by year, in the place which Jehovah doth choose, thou and thy house.
Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
21 'And when there is in it a blemish, lame, or blind, any evil blemish, thou dost not sacrifice it to Jehovah thy God;
Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
22 within thy gates thou dost eat it, the unclean and the clean alike, as the roe, and as the hart.
Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
23 Only, its blood thou dost not eat; on the earth thou dost pour it as water.
Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.