< Amos 7 >

1 Thus hath the Lord Jehovah shewed me, and lo, He is forming locusts at the beginning of the ascending of the latter growth, and lo, the latter growth [is] after the mowings of the king;
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 and it hath come to pass, when it hath finished to consume the herb of the land, that I say: 'Lord Jehovah, forgive, I pray Thee, How doth Jacob arise — for he [is] small?'
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 Jehovah hath repented of this, 'It shall not be,' said Jehovah.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Thus hath the Lord Jehovah shewed me, and lo, the Lord Jehovah is calling to contend by fire, and it consumeth the great deep, yea, it hath consumed the portion, and I say:
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 'Lord Jehovah, cease, I pray Thee, How doth Jacob arise — for he [is] small?'
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 Jehovah hath repented of this, 'It also shall not be,' said the Lord Jehovah.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Thus hath He shewed me, and lo, the Lord is standing by a wall [made according to] a plumb-line, and in His hand a plumb-line;
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 and Jehovah saith unto me, 'What art thou seeing, Amos?' And I say, 'A plumb-line;' and the Lord saith: 'Lo, I am setting a plumb-line in the midst of My people Israel, I do not add any more to pass over to it.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 And desolated have been high places of Isaac, And sanctuaries of Israel are wasted, And I have risen against the house of Jeroboam with a sword.'
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 And Amaziah priest of Beth-El sendeth unto Jeroboam king of Israel, saying, 'Amos hath conspired against thee in the midst of the house of Israel; the land is not able to bear all his words,
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 for thus said Amos: By sword die doth Jeroboam, And Israel certainly removeth from off its land.'
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 And Amaziah saith unto Amos, 'Seer, go flee for thee unto the land of Judah, and eat there bread, and there thou dost prophesy;
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 and [at] Beth-El do not add to prophesy any more, for it [is] the king's sanctuary, and it [is] the royal house.'
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 And Amos answereth and saith unto Amaziah, 'I [am] no prophet, nor a prophet's son [am] I, but a herdsman I [am], and a cultivator of sycamores,
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 and Jehovah taketh me from after the flock, and Jehovah saith unto me, Go, prophesy unto My people Israel.
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 And now, hear a word of Jehovah: thou art saying, Do not prophesy against Israel, nor drop [any thing] against the house of Isaac,
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 therefore thus said Jehovah: Thy wife in the city doth go a-whoring, And thy sons and thy daughters by sword do fall, And thy land by line is apportioned, And thou on an unclean land diest, And Israel certainly removeth from off its land.'
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amos 7 >