< 2 Samuel 23 >

1 And these [are] the last words of David: — 'The affirmation of David son of Jesse — And the affirmation of the man raised up — Concerning the Anointed of the God of Jacob, And the Sweetness of the Songs of Israel:
Nawa mawu otsiriza a Davide: “Mawu a Davide mwana wa Yese, mawu a munthu amene wakwezedwa ndi Wammwambamwamba, munthu wodzozedwa ndi Mulungu wa Yakobo, woyimba nyimbo za Israeli:
2 The Spirit of Jehovah hath spoken by me, And His word [is] on my tongue.
“Mzimu wa Yehova unayankhula kudzera mwa ine; mawu ake anali pakamwa panga.
3 He said — the God of Israel — to me, He spake — the Rock of Israel: He who is ruling over man [is] righteous, He is ruling in the fear of God.
Mulungu wa Israeli anayankhula, Thanthwe la Israeli linati kwa ine: ‘Pamene munthu alamulira anthu mwachilungamo, pamene alamulira moopa Mulungu,
4 And as the light of morning he riseth, A morning sun — no clouds! By the shining, by the rain, Tender grass of the earth!
amakhala ngati kuwala kwa mmamawa, mmawa wopanda mitambo, monga kuwala pamene mvula yaleka kugwa imene imameretsa udzu mʼnthaka.’
5 For — not so [is] my house with God; For — a covenant age-during He made with me, Arranged in all things, and kept; For — all my salvation, and all desire, For — He hath not caused [it] to spring up.
“Kodi banja langa silolungama pamaso pa Mulungu? Kodi Iye sanachite pangano losatha ndi ine, lokonzedwa ndi lotetezedwa mbali zonse? Kodi sadzakwaniritsa chipulumutso changa, ndi kundipatsa chokhumba changa chilichonse?
6 As to the worthless — As a thorn driven away [are] all of them, For — not by hand are they taken;
Koma anthu oyipa ndiwo ayenera kutayidwa kunja ngati minga, imene sitengedwa ndi manja.
7 And the man who cometh against them Is filled with iron and the staff of a spear, And with fire they are utterly burnt In the cessation.'
Aliyense amene wayikhudza mingayo amayidula pogwiritsa ntchito chigwandali kapena ndodo ya mkondo; nayitentha pa moto.”
8 These [are] the names of the mighty ones whom David hath: sitting in the seat [is] the Tachmonite, head of the captains — he [is] Adino, who hardened himself against eight hundred — wounded at one time.
Nawa mayina a ankhondo amphamvu a Davide: Yosebu-Basebeti wa ku Takemoni mkulu wa atsogoleri a ankhondo atatu. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 800 nthawi imodzi.
9 And after him [is] Eleazar son of Dodo, son of Ahohi, of the three mighty men with David; in their exposing themselves among the Philistines — they have been gathered there to battle, and the men of Israel go up —
Wotsatana naye anali Eliezara mwana wa Dodo Mwahohi. Monga mmodzi mwa ankhondo atatu amphamvu a Davide, iye anali ndi Davide pamene anazunza Afilisti amene anasonkhana ku Pasi-Damimu kuchita nkhondo. Kenaka ankhondo a Israeli anabwerera mʼmbuyo.
10 he hath arisen, and smiteth among the Philistines till that his hand hath been weary, and his hand cleaveth unto the sword, and Jehovah worketh a great salvation on that day, and the people turn back after him only to strip off.
Koma iye anayima osasuntha ndipo anakantha Afilisti mpaka mkono wake unatopa ndipo unakanirira ku lupanga lake. Yehova anapereka chigonjetso chachikulu pa tsiku limenelo. Asilikali anabwerera kwa Eliezara, kukatenga katundu wa anthu ophedwa.
11 And after him [is] Shammah son of Agee the Hararite, and the Philistines are gathered into a company, and there is there a portion of the field full of lentiles, and the people hath fled from the presence of the Philistines,
Wotsatana naye anali Sama mwana wa Age Mharari. Pamene Afilisti anasonkhana pamalo pamene panali munda wa mphodza, ankhondo a Israeli anathawa Afilistiwo.
12 and he stationeth himself in the midst of the portion, and delivereth it, and smiteth the Philistines, and Jehovah worketh a great salvation.
Koma Sama anayima pakati pa mundawo. Iye anawuteteza nakantha Afilistiwo ndipo Yehova anawapambanitsa koposa.
13 And three of the thirty heads go down and come unto the harvest, unto David, unto the cave of Adullam, and the company of the Philistines are encamping in the valley of Rephaim,
Pa nthawi yokolola, atatu mwa atsogoleri makumi atatu anabwera kwa Davide ku phanga la Adulamu, pamene gulu la Afilisti linali litamanga misasa mʼchigwa cha Refaimu.
14 and David [is] then in a fortress, and the station of the Philistines [is] then in Beth-Lehem,
Nthawi imeneyo Davide anali mu linga, ndipo boma la Afilisti linali ku Betelehemu.
15 and David longeth and saith, 'Who doth give me a drink of the water of the well of Beth-Lehem, which [is] by the gate?'
Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”
16 And the three mighty ones cleave through the camp of the Philistines, and draw water out of the well of Beth-Lehem, which [is] by the gate, and take [it] up, and bring in unto David; and he was not willing to drink it, and poureth it out to Jehovah,
Choncho anthu amphamvu atatuwa anadutsa mizere ya Afilisti, natunga madzi amene anali mʼchitsime chomwe chinali pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu nabwera nawo kwa Davide. Koma iye anakana kumwa. Mʼmalo mwake anathira pansi pamaso pa Yehova.
17 and saith, 'Far be it from me, O Jehovah, to do this; is it the blood of the men who are going with their lives?' and he was not willing to drink it; these [things] did the three mighty ones.
Iye anati, “Inu Yehova, musalole kuti ine ndichite chinthu ichi! Kodi awa si magazi a anthu amene anayika miyoyo yawo pachiswe?” Ndipo Davide sanamwe madziwo. Zimenezi ndi zimene anachita anthu amphamvu atatuwo.
18 And Abishai brother of Joab, son of Zeruiah, he [is] head of three, and he is lifting up his spear against three hundred — wounded, and he hath a name among three.
Abisai mʼbale wa Yowabu mwana wa Zeruya ndiye anali mtsogoleri wa anthu atatuwa. Iye anapha ndi mkondo ankhondo 300, choncho iyeyo anali wotchuka pakati pa anthu atatu aja.
19 Of the three is he not the honoured? and he becometh their head; and unto the [first] three he hath not come.
Kodi iyeyo sanali wolemekezeka koposa? Iye anakhala mtsogoleri wawo ngakhale kuti sanali mʼgulu la anthu atatu aja.
20 And Benaiah son of Jehoiada (son of a man of valour, great in deeds from Kabzeel), he hath smitten two lion-like men of Moab, and he hath gone down and smitten the lion in the midst of the pit in a day of snow.
Benaya mwana wa Yehoyada wa ku Kabizeeli anali munthu wolimba mtima amene anachita zinthu zamphamvu. Iye anakantha ankhondo awiri otchuka a ku Mowabu. Tsiku lina kukuzizira kwambiri, iye analowa mʼdzenje ndi kuphamo mkango.
21 And he hath smitten the Egyptian man, a man of appearance, and in the hand of the Egyptian [is] a spear, and he goeth down unto him with a rod, and taketh violently away the spear out of the hand of the Egyptian, and slayeth him with his own spear.
Ndipo iye anakanthanso Mwigupto wamkulu msinkhu. Ngakhale kuti Mwiguptoyo anali ndi mkondo mʼdzanja mwake, Benaya anapita kukamenyana naye ali ndi chibonga chokha mʼmanja. Iye analanda mkondo mʼdzanja la Mwiguptoyo ndi kumupha ndi mkondo wake womwe.
22 These [things] hath Benaiah son of Jehoiada done, and hath a name among three mighty.
Izi ndi zamphamvu zimene Benaya mwana wa Yehoyada anachita. Iyeyo analinso wotchuka ngati anthu atatu amphamvu aja.
23 Of the thirty he is honoured, and unto the three he came not; and David setteth him over his guard.
Iye ankalemekezedwa kuposa wina aliyense mwa anthu makumi atatu aja, koma sanali mʼgulu la anthu atatu aja. Ndipo Davide anamuyika kukhala woyangʼanira asilikali omuteteza.
24 Asahel brother of Joab [is] of the thirty; Elhanan son of Dodo of Beth-Lehem.
Mʼgulu la anthu makumi atatu aja munalinso awa: Asaheli mʼbale wa Yowabu, Elihanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,
25 Shammah the Harodite, Elika the Harodite,
Sama Mharodi, Elika Mherodi,
26 Helez the Paltite, Ira son of Ikkesh the Tekoite,
Helezi Mpaliti, Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa,
27 Abiezer the Annethothite, Mebunnai the Hushathite,
Abiezeri wa ku Anatoti, Sibekai Mhusati,
28 Zalmon the Ahohite, Maharai the Netophathite,
Zalimoni Mwahohi, Maharai Mnetofa,
29 Heleb son of Baanah the Netophathite, Ittai son of Ribai from Gibeah of the sons of Benjamin,
Heledi mwana wa Baana Mnetofa, Itai mwana wa Ribai wa ku Gibeya ku Benjamini,
30 Benaiah the Pirathonite, Hiddai of the brooks of Gaash,
Benaya Mpiratoni, Hidayi wa ku zigwa za Gaasi.
31 Abi-Albon the Arbathite, Azmaveth the Barhumite,
Abi-Aliboni Mwaribati, Azimaveti Mbarihumi,
32 Eliahba the Shaalbonite, [of] the sons of Jashen, Jonathan,
Eliyahiba Msaaliboni, ana a Yaseni, Yonatani,
33 Shammah the Hararite, Ahiam son of Sharar the Hararite,
mwana wa Sama Mharari, Ahiamu mwana wa Sarari Mharari,
34 Eliphelet son of Ahasbai, son of the Maachathite, Eliam son of Ahithophel the Gilonite,
Elifeleti mwana wa Ahasibai Mmaakati, Eliamu mwana wa Ahitofele Mgiloni,
35 Hezrai the Carmelite, Paarai the Arbite,
Heziro wa ku Karimeli, Paarai Mwaribi,
36 Igal son of Nathan from Zobah, Bani the Gadite,
Igala mwana wa Natani wa ku Zoba, mwana wa Hagiri,
37 Zelek the Ammonite, Naharai the Beerothite, bearer of the weapons of Joab son of Zeruiah,
Zeleki Mwamoni, Naharai wa ku Beeroti, mnyamata wonyamula zida za Yowabu mwana wa Zeruya,
38 Ira the Ithrite, Gareb the Ithrite,
Ira Mwitiri, Garebu Mwitiri,
39 Uriah the Hittite; in all thirty and seven.
ndi Uriya Mhiti. Onse pamodzi analipo 37.

< 2 Samuel 23 >