< 2 Chronicles 10 >

1 And Rehoboam goeth to Shechem, for [to] Shechem have all Israel come to cause him to reign.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
2 And it cometh to pass, at Jeroboam son of Nebat's — who [is] in Egypt because he hath fled from the face of Solomon the king — hearing, that Jeroboam turneth back out of Egypt;
Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
3 and they send and call for him, and Jeroboam cometh in, and all Israel, and speak unto Rehoboam, saying,
Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
4 'Thy father made our yoke sharp, and now, make light [somewhat] of the sharp service of thy father, and of his heavy yoke that he put upon us, and we serve thee.'
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
5 And he saith unto them, 'Yet three days — then return ye unto me;' and the people go.
Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
6 And king Rehoboam consulteth with the aged men who have been standing before Solomon his father in his being alive, saying, 'How are ye counselling to answer this people?'
Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
7 And they speak unto him, saying, 'If thou dost become good to this people, and hast been pleased with them, and spoken unto them good words, then they have been to thee servants all the days.'
Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
8 And he forsaketh the counsel of the aged men that they counselled him, and consulteth with the lads who have grown up with him, those standing before him,
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
9 and he saith unto them, 'What are ye counselling, and we answer this people that have spoken unto me, saying, Make light [somewhat] of the yoke that thy father put upon us?'
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
10 And the lads who have grown up with him, speak with him, saying, 'Thus dost thou say to the people who have spoken unto thee, saying, Thy father made our yoke heavy, and thou, make light [somewhat] of our yoke; thus dost thou say unto them, My little finger is thicker than the loins of my father;
Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
11 and now, my father laid on you a heavy yoke, and I — I add unto your yoke; my father chastised you with whips, and I — with scorpions.'
Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 And Jeroboam cometh in, and all the people, unto Rehoboam on the third day, as the king spake, saying, 'Return unto me on the third day.'
Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
13 And the king answereth them sharply, and king Rehoboam forsaketh the counsel of the aged men,
Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
14 and speaketh unto them according to the counsel of the lads, saying, 'My father made your yoke heavy, and I — I add unto it; my father chastised you with whips, and I — with scorpions.'
Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 And the king hath not hearkened unto the people, for the revolution hath been from God, for the sake of Jehovah's establishing His word that He spake by the hand of Abijah the Shilonite unto Jeroboam son of Nebat.
Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 And all Israel have seen that the king hath not hearkened to them, and the people send back [to] the king, saying, 'What portion have we in David? yea, there is no inheritance in a son of Jesse; each to thy tents, O Israel; now, see thy house — David,' and all Israel go to their tents.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
17 As to the sons of Israel who are dwelling in the cities of Judah — Rehoboam reigneth over them.
Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
18 And king Rehoboam sendeth Hadoram, who [is] over the tribute, and the sons of Israel cast at him stones, and he dieth; and king Rehoboam hath strengthened himself to go up into a chariot to flee to Jerusalem;
Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
19 and Israel transgress against the house of David unto this day.
Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.

< 2 Chronicles 10 >