< 1 Samuel 9 >

1 And there is a man of Benjamin, and his name [is] Kish, son of Abiel, son of Zeror, son of Bechorath, son of Aphiah, a Benjamite, mighty of valour,
Panali munthu wina wa fuko la Benjamini, wotchuka, dzina lake Kisi, mwana wa Abieli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya.
2 and he hath a son, and his name [is] Saul, a choice youth and goodly, and there is not a man among the sons of Israel goodlier than he — from his shoulder and upward, higher than any of the people.
Iyeyu anali ndi mwana dzina lake Sauli, mnyamata wa maonekedwe abwino. Pakati pa Aisraeli onse panalibe wofanana naye. Anali wamtali kotero kuti anthu onse ankamulekeza mʼmapewa.
3 And the asses of Kish, father of Saul, are lost, and Kish saith unto Saul his son, 'Take, I pray thee, with thee, one of the young men, and rise, go, seek the asses.'
Tsono abulu a Kisi, abambo ake a Sauli anasowa. Choncho Kisi anati kwa mwana wake Sauli, “Tenga wantchito mmodzi ndipo mupite mukafunefune abuluwo.”
4 And he passeth over through the hill-country of Ephraim, and passeth over through the land of Shalisha, and they have not found; and they pass over through the land of Shaalim, and they are not; and he passeth over through the land of Benjamin, and they have not found.
Choncho iwo anadutsa dziko la mapiri a Efereimu ndi dera la Salisa, koma sanawapeze. Anadutsa ku Saalimu koma abuluwo sanawapeze. Kenaka anadutsa dziko la Benjamini, koma osawapezabe.
5 They have come in unto the land of Zuph, and Saul hath said to his young man who [is] with him, 'Come, and we turn back, lest my father leave off from the asses, and hath been sorrowful for us.'
Atafika ku dera la Zufi, Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Tiye tibwerere, mwina abambo anga angasiye kudandaula za abulu ndipo adzayamba kudandaula za ife.”
6 And he saith to him, 'Lo, I pray thee, a man of God [is] in this city, and the man is honoured; all that he speaketh doth certainly come; now, we go there, it may be he doth declare to us our way on which we have gone.'
Koma mnyamatayo anayankha kuti, “Taonani, mu mzinda uwo muli munthu wa Mulungu. Anthu amamupatsa ulemu kwambiri, ndipo zonse zimene amanena zimachitika. Tiyeni tipite kumeneko tsopano. Mwina adzatiwuza kumene tiyenera kulowera.”
7 And Saul saith to his young man, 'And lo, we go, and what do we bring in to the man? for the bread hath gone from our vessels, and a present there is not to bring in to the man of God — what [is] with us?'
Sauli anafunsa mnyamata wake kuti, “Tikapita tikamupatsa chiyani munthuyo pakuti chakudya chimene chinali mʼmatumba mwathu chatha? Tilibe mphatso iliyonse yoti timutengere munthu wa Mulungu. Nanga tili ndi chiyani?”
8 And the young man addeth to answer Saul, and saith, 'Lo, there is found with me a fourth of a shekel of silver: and I have given to the man of God, and he hath declared to us our way.'
Mnyamatayo anayankha kuti, “Onani, ndili ndi kandalama kakangʼono ka siliva. Ndikamupatsa munthu wa Mulunguyo ndipo akatidziwitsa kumene kuli abuluwo.”
9 Formerly in Israel, thus said the man in his going to seek God, 'Come and we go unto the seer,' for the 'prophet' of to-day is called formerly 'the seer.'
(Kale mu Israeli ngati munthu afuna kukapempha nzeru kwa Mulungu ankanena kuti, “Tiyeni tipite kwa mlosi.” Ndiye kuti munthu amene lero akutchedwa mneneri, kale ankatchedwa mlosi).
10 And Saul saith to his young man, 'Thy word [is] good; come, we go;' and they go unto the city where the man of God [is].
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake kuti, “Chabwino, tiye tipite.” Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda umene kunali munthu wa Mulunguyo.
11 They are going up in the ascent of the city, and have found young women going out to draw water, and say to them, 'Is the seer in this [place]?'
Akukwera phiri kupita ku mzindawo anakumana ndi atsikana akutuluka mu mzindamo kukatunga madzi, ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mlosi uja alipo?”
12 And they answer them and say, 'He is; lo, before thee! haste, now, for to-day he hath come in to the city, for the people hath a stated sacrifice in a high place.
Iwo anayankha, “Inde alipo. Ali kutsogolo kwanuku, fulumirani tsopano, wangobwera kumene mu mzinda wathu uno lero, chifukwa lero anthu akupereka nsembe ku phiri.
13 At your going in to the city so ye do find him, before he doth go up in to the high place to eat; for the people do not eat till his coming, for he doth bless the sacrifice; afterwards they eat, who are called, and now, go up, for at this time ye find him.'
Mukangolowa mu mzindawo mumupeza asanapite ku phiri kukadya. Anthu sangayambe kudya iye asanabwere chifukwa iyeyu ayenera kudalitsa nsembeyo. Kenaka anthu oyitanidwa adzayamba kudya. Pitani tsopano, chifukwa muyenera kumupeza nthawi ino.”
14 And they go up in to the city; they are coming in to the midst of the city, and lo, Samuel is coming out to meet them, to go up to the high place;
Choncho anapita ku mzinda kuja. Akulowa mu mzindamo, anaona Samueli akutuluka mu mzindamo akubwera kumene kunali iwo, koma amapita ku phiri, ku malo wopatulika.
15 and Jehovah had uncovered the ear of Samuel one day before the coming of Saul, saying,
Koma chadzulo lake Sauli asanafike, Yehova anali atamuwuza kale Samueli za zimenezi kuti,
16 'At this time tomorrow, I send unto thee a man out of the land of Benjamin — and thou hast anointed him for leader over My people Israel, and he hath saved My people out of the hand of the Philistines; for I have seen My people, for its cry hath come in unto Me.'
“Mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzakutumizira munthu wochokera ku dziko la Benjamini. Udzamudzoze kuti akhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. Iye adzawapulumutsa mʼdzanja la Afilisti. Ine ndaona kuzunzika kwawo ndipo ndamva kulira kwawo.”
17 When Samuel hath seen Saul, then hath Jehovah answered him, 'Lo, the man of whom I have spoken unto thee; this [one] doth restrain My people.'
Samueli atamuona Sauli, Yehova anamuwuza kuti, “Munthu ndinakuwuza uja ndi uyu. Iyeyu adzalamulira anthu anga.”
18 And Saul draweth nigh to Samuel in the midst of the gate, and saith, 'Declare, I pray thee, to me, where [is] this — the seer's house?'
Tsono Sauli anayandikira Samueli pa chipata ndipo anamufunsa, “Kodi mungandiwuze kumene kuli nyumba ya mlosi?”
19 And Samuel answereth Saul and saith, 'I [am] the seer; go up before me into the high place, and ye have eaten with me to-day, and I have sent thee away in the morning, and all that [is] in thy heart I declare to thee.
Samueli anayankha, “Ine ndine mlosiyo. Tsogolani kupita ku phiri pakuti lero mudya ndi ine, ndipo mawa mmawa ndidzakuwuzani zonse zimene zili mu mtima mwanu.
20 As to the asses which are lost to thee this day three days, set not thy heart to them, for they have been found; and to whom [is] all the desire of Israel?' is it not to thee and to all thy father's house?'
Musadere nkhawa za abulu anu amene akhala akusowa masiku atatu apitawa, poti apezeka kale. Kodi Aisraeli onse akufunitsitsa ndani? Kodi si ndiwe ndi nyumba yonse ya abambo ako?”
21 And Saul answereth and saith, 'Am not I a Benjamite — of the smallest of the tribes of Israel? and my family the least of all the families of the tribe of Benjamin? and why hast thou spoken unto me according to this word?'
Sauli anayankha, “Inetu ndine Mbenjamini, fuko lalingʼono la mafuko onse a Israeli, ndipo banja langa ndi lalingʼono pakati pa mabanja a fuko la Benjamini. Nanga nʼchifukwa chiyani mukunena zimenezi kwa ine?”
22 And Samuel taketh Saul, and his young man, and bringeth them in to the chamber, and giveth to them a place at the head of those called; and they [are] about thirty men.
Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wake uja ndi kulowa nawo mʼchipinda chachikulu ndipo anawakhazika kutsogolo kwa anthu oyitanidwa. Onse pamodzi analipo anthu makumi atatu.
23 And Samuel saith to the cook, 'Give the portion which I gave to thee, of which I said unto thee, 'Set it by thee?'
Tsono Samueli anati kwa wophika, “Bwera nayo nyama imene ndinakupatsa, imene ndinakuwuza kuti uyisunge pambali.”
24 (and the cook lifteth up the leg, and that which [is] on it, and setteth before Saul), and he saith, 'Lo, that which is left; set [it] before thee — eat, for to this appointed season it is kept for thee, saying, The people I have called;' and Saul eateth with Samuel on that day.
Kotero wophikayo anatenga mwendo wa nyama ndipo anawuyika patsogolo pa Sauli. Samueli anati “Nayi nyama imene ndinakusungira kuti pa nthawi yake udye pamodzi ndi anthu amene ndawayitana.” Ndipo Sauli anadya tsiku limenelo ndi Samueli.
25 And they come down from the high place to the city, and he speaketh with Saul on the roof.
Atatsika kuchoka ku phiri kuja, Samueli anamukonzera Sauli malo ogona pa denga la nyumba yake, ndipo Sauli anagona pamenepo.
26 And they rise early, and it cometh to pass, at the ascending of the dawn, that Samuel calleth unto Saul, on the roof, saying, 'Rise, and I send thee away;' and Saul riseth, and they go out, both of them — he and Samuel, without.
Tsono mʼbandakucha Samueli anayitana Sauli pa dengapo nati, “Konzeka ndipo ine ndikuperekeza.” Choncho Sauli anadzuka ndipo onse awiri, Samueli ndi Sauli anakalowa mu msewu.
27 They are going down in the extremity of the city, and Samuel hath said unto Saul, 'Say to the young man that he pass on before us (and he passeth on), and thou, stand at this time, and I cause thee to hear the word of God.'
Atakafika ku mathero a mzindawo, Samueli anati kwa Sauli, “Muwuzeni mnyamata wanu kuti atsogole, koma inuyo muyime pangʼono kuti ndikuwuzeni mawu ochokera kwa Mulungu.”

< 1 Samuel 9 >