< 1 Samuel 6 >

1 And the ark of Jehovah is in the field of the Philistines seven months,
Bokosi la Yehova linakhala mʼdziko la Afilisti kwa miyezi isanu ndi iwiri.
2 and the Philistines call for priests and for diviners, saying, 'What do we do to the ark of Jehovah? let us know wherewith we send it to its place?'
Tsono Afilisti anayitana ansembe ndi amawula ndipo anati, “Tichite nalo chiyani Bokosi la Yehova? Tiwuzeni momwe tidzalitumizira ku malo ake.”
3 And they say, 'If ye are sending away the ark of the God of Israel, ye do not send it away empty; for ye do certainly send back to Him a guilt-offering; then ye are healed, and it hath been known to you why His hand doth not turn aside from you.'
Iwo anayankha kuti, “Ngati mufuna kubweza Bokosi la Mulungu wa Israeli, musalitumize wopanda kanthu, koma muyesetse kulitumiza pamodzi ndi nsembe yopepesera machimo. Mukatero mudzachiritsidwa, ndipo mudzadziwa chifukwa chiyani chilango cha Yehova sichikukuchokani.”
4 And they say, 'What [is] the guilt-offering which we send back to Him?' and they say, 'The number of the princes of the Philistines — five golden emerods, and five golden mice — for one plague [is] to you all, and to your princes,
Afilisti anafunsanso kuti “Kodi ife tipereke nsembe yanji yopepesera machimo?” Iwo anayankha kuti, “Mupereke zifanizo zagolide za zithupsa zisanu ndi zamakoswe asanu malingana ndi chiwerengero cha akalonga a Afilisti popeza mliri womwewo wagwera inu ndi akalonga anu.
5 and ye have made images of your emerods, and images of your mice that are corrupting the land, and have given honour to the God of Israel; it may be He doth lighten His hand from off you, and from off your gods, and from off your land;
Mupange zifanizo za zithupsa zisanu ndi za makoswe asanu amene akuwononga dziko lanu ndipo mupereke ulemu kwa Israeli. Mwina adzaleka kuzunza inu, milungu yanu ndi dziko lanu.
6 and why do ye harden your heart as the Egyptians and Pharaoh hardened their heart? do they not — when He hath rolled Himself upon them — send them away, and they go?
Nʼchifukwa chiyani mukuwumitsa mitima monga anachita Aigupto ndi Farao? Mulungu atawalanga anthu a ku Igupto aja kodi suja anawalola Aisraeli kuti azipita ndipo anapitadi?
7 'And now, take and make one new cart, and two suckling kine, on which a yoke hath not gone up, and ye have bound the kine in the cart, and caused their young ones to turn back from after them to the house,
“Tsopano konzani galeta latsopano limodzi ndiponso ngʼombe ziwiri zazikazi zamkaka zimene sizinavalepo goli. Muzimangirire ngʼombezo ku ngoloyo, koma ana awo muwachotse ndi kuwasiya kwanu.
8 and ye have taken the ark of Jehovah, and put it on the cart, and the vessels of gold which ye have returned to Him — a guilt-offering — ye put in a coffer on its side, and have sent it away, and it hath gone;
Mutenge Bokosi la Yehova ndi kuliyika pa galetapo ndipo pambali pake pakhale Bokosi, mʼmene muyikemonso zinthu zagolide zomwe mukutumiza kwa Iye monga nsembe yopepesera machimo. Kenaka, mulisiye lizipita.
9 and ye have seen, if the way of its own border it goeth up to Beth-Shemesh — He hath done to us this great evil; and if not, then we have known that His hand hath not come against us; an accident it hath been to us.'
Koma muziliyangʼana. Ngati lilondola njira yopita kwawo kwa Bokosilo mpaka ku Beti-Semesi ndiye kuti amene watichita zoyipa zazikulu zoterezi ndi Mulungu wa Israeli. Koma ngati silitero, ife tidzadziwa kuti sanali Mulungu wa Israeli amene watizunza koma kuti zinangochitika mwatsoka.”
10 And the men do so, and take two suckling kine, and bind them in the cart, and their young ones they have shut up in the house;
Anthu aja anachitadi zimenezi. Anatenga ngʼombe zamkaka ziwiri nazimanga ku galeta lija. Koma ana awo anawatsekera mʼkhola.
11 and they place the ark of Jehovah upon the cart, and the coffer, and the golden mice, and the images of their emerods.
Tsono anayika Bokosi la Yehova pa galeta pamodzi ndi bokosi limene munali makoswe agolide ndi zifanizo zawo za zithupsa.
12 And the kine go straight in the way, on the way to Beth-Shemesh, in one highway they have gone, going and lowing, and have not turned aside right or left; and the princes of the Philistines are going after them unto the border of Beth-Shemesh.
Ngʼombe zija zinapita molunjika kutsata msewu wopita ku Beti Semesi zikulira njira yonse. Sizinakhotere kumanja kapena kumanzere. Akalonga a Afilisti anazitsatira mpaka mʼmalire a Beti-Semesi.
13 And the Beth-Shemeshites are reaping their wheat-harvest in the valley, and they lift up their eyes, and see the ark, and rejoice to see [it].
Nthawi imeneyi anthu a ku Beti-Semesi amakolola tirigu mʼchigwa ndipo pamene anayangʼana ndi kuona Bokosi la Chipangano likubwera anakondwa.
14 And the cart hath come in unto the field of Joshua the Beth-Shemeshite, and standeth there, and there [is] a great stone, and they cleave the wood of the cart, and the kine they have caused to ascend — a burnt-offering to Jehovah.
Galeta lija linafika ku munda wa Yoswa ku Beti-Semesi ndipo linayima. Kumeneko kunali mwala waukulu. Tsono anthu anawaza nkhuni galetalo, ndipo anapha ngʼombe zija ndi kuzipereka ngati nsembe zopsereza kwa Yehova.
15 And the Levites have taken down the ark of Jehovah, and the coffer which [is] with it, in which [are] the vessels of gold, and place [them] on the great stone; and the men of Beth-Shemesh have caused to ascend burnt-offerings and sacrifice sacrifices in that day to Jehovah;
Alevi nʼkuti atatsitsa Bokosi la Yehova, pamodzi ndi bokosi mmene munali zinthu zagolide, ndipo anawayika pa mwala uja waukulu. Tsiku limenelo anthu a ku Beti-Semesi anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa Yehova.
16 and the five princes of the Philistines have seen [it], and turn back [to] Ekron, on that day.
Atsogoleri asanu a Afilisti ataona izi anabwerera ku Ekroni tsiku lomwelo.
17 And these [are] the golden emerods which the Philistines have sent back — a guilt-offering to Jehovah: for Ashdod one, for Gaza one, for Ashkelon one, for Gath one, for Ekron one;
Zifanizo zagolide za zithupsa zimene Afilisti anatumiza ngati nsembe zopepesera machimo kwa Yehova zinkayimirira mizinda isanu iyi motere: chimodzi cha ku Asidodi, china cha ku Gaza ndi zina za ku Asikeloni, Gati ndi Ekroni.
18 and the golden mice — the number of all the cities of the Philistines — for the five princes, from the fenced city even unto the hamlet of the villages, even unto the great meadow on which they placed the ark of Jehovah — [are] unto this day in the field of Joshua the Beth-Shemeshite.
Ndipo chiwerengero cha zifanizo za makoswe chinali chofanana ndi chiwerengero cha mizinda ya akalonga asanu a Afilisti. Mizindayi inali yotetezedwa bwino ndi ina yapamtetete. Mwala waukulu umene anayikapo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼmunda mwa Yoswa ku Beti-Semesi uli ngati mboni mpaka lero.
19 And He smiteth among the men of Beth-Shemesh, for they looked into the ark of Jehovah, yea, He smiteth among the people seventy men — fifty chief men; and the people mourn, because Jehovah smote among the people — a great smiting.
Yehova anakantha amuna a ku Beti-Semesi 70 chifukwa anasuzumira mʼBokosi la Chipangano cha Yehova. Ndipo anzawo analira chifukwa Yehova anawalanga kwambiri.
20 And the men of Beth-Shemesh say, 'Who is able to stand before Jehovah, this holy God? and unto whom doth He go up from us?'
Tsono anthu a ku Beti-Semesi anafunsa, “Ndani angathe kuyima pamaso pa Yehova Mulungu Woyera? Bokosi la Chipanganoli lipita kuti likachoka pano?”
21 And they send messengers unto the inhabitants of Kirjath-Jearim, saying, 'The Philistines have sent back the ark of Jehovah; come down, take it up unto you.'
Tsono iwo anatumiza a mithenga kwa anthu a ku Kiriati-Yearimu kuti, “Afilisti atibwezera Bokosi la Yehova. Bwerani kuno mudzalitenge, mupite nalo kwanuko.”

< 1 Samuel 6 >